< Yesaya 49 >
1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
to hear: hear coastland to(wards) me and to listen people from distant LORD from belly: womb to call: call to me from belly mother my to remember name my
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
and to set: make lip my like/as sword sharp in/on/with shadow hand his to hide me and to set: make me to/for arrow to purify in/on/with quiver his to hide me
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
and to say to/for me servant/slave my you(m. s.) Israel which in/on/with you to beautify
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
and I to say to/for vain be weary/toil to/for formlessness and vanity strength my to end: expend surely justice my with LORD and wages my with God my
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
and now to say LORD to form: formed me from belly: womb to/for servant/slave to/for him to/for to return: return Jacob to(wards) him and Israel (to/for him *Q(K)*) to gather and to honor: honour in/on/with eye LORD and God my to be strength my
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
and to say to lighten from to be you to/for me servant/slave to/for to arise: establish [obj] tribe Jacob (and to watch *Q(K)*) Israel to/for to return: return and to give: make you to/for light nation to/for to be salvation my till end [the] land: country/planet
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
thus to say LORD to redeem: redeem Israel holy his to/for to despise soul: person to/for to abhor nation to/for servant/slave to rule king to see: see and to arise: rise ruler and to bow because LORD which be faithful holy Israel and to choose you
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
thus to say LORD in/on/with time acceptance to answer you and in/on/with day salvation to help you and to watch you and to give: give you to/for covenant people to/for to arise: establish land: country/planet to/for to inherit inheritance be desolate: destroyed
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
to/for to say to/for to bind to come out: come to/for which in/on/with darkness to reveal: uncover upon way: road to pasture and in/on/with all bareness pasturing their
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
not be hungry and not to thirst and not to smite them scorching and sun for to have compassion them to lead them and upon spring water to guide them
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
and to set: make all mountain: mount my to/for way: road and highway my to exalt [emph?]
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
behold these from distant to come (in): come and behold these from north and from sea: west and these from land: country/planet Syene
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
to sing heaven and to rejoice land: country/planet (and to break out *Q(K)*) mountain: mount cry for to be sorry: comfort LORD people his and afflicted his to have compassion
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
and to say Zion to leave: forsake me LORD and Lord to forget me
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
to forget woman infant her from to have compassion son: child belly: womb her also these to forget and I not to forget you
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
look! upon palm to decree you wall your before me continually
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
to hasten son: child your to overthrow you and to destroy you from you to come out: come
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
to lift: look around eye your and to see: see all their to gather to come (in): come to/for you alive I utterance LORD for all their like/as ornament to clothe and to conspire them like/as daughter-in-law: bride
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
for desolation your and be desolate: destroyed your and land: country/planet ruins your for now be distressed from to dwell and to remove to swallow up you
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
still to say in/on/with ear your son: child bereavement your narrow to/for me [the] place to approach: approach [emph?] to/for me and to dwell
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
and to say in/on/with heart your who? to beget to/for me [obj] these and I childless and solitary to reveal: remove and to turn aside: remove and these who? to magnify look! I to remain to/for alone me these where? they(masc.)
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
thus to say Lord YHWH/God behold to lift: raise to(wards) nation hand my and to(wards) people to exalt ensign my and to come (in): bring son: child your in/on/with bosom and daughter your upon shoulder to lift: bear
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
and to be king be faithful you and princess their to suckle your face land: soil to bow to/for you and dust foot your to lick and to know for I LORD which not be ashamed to await me
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
to take: take from mighty man prey and if captivity righteous to escape
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
for thus to say LORD also captivity mighty man to take: take and prey ruthless to escape and with opponent your I to contend and [obj] son: child your I to save
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
and to eat [obj] to oppress you [obj] flesh their and like/as sweet blood their be drunk [emph?] and to know all flesh for I LORD to save you and to redeem: redeem your mighty Jacob