< Yesaya 49 >
1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Hearken, O isles, unto me; and listen, ye people, from afar: The Lord hath called me from my birth; from my mother's womb hath he made mention of my name.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
And he hath rendered my mouth like a sharp sword; in the shadow of his hand hath he hidden me: and he hath rendered me as a polished arrow; in his quiver hath he concealed me;
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
And said unto me, My servant art thou, O Israel, thou on whom I will be glorified.
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
But I had indeed said, For no purpose have I labored, for naught and vanity have I spent my strength; yet surely my cause is with the Lord, and the recompense of my work with my God.
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
And now hath said the Lord that formed me from the womb to be his servant, to bring Jacob again to him, that Israel may be gathered unto him, that I should be honored in the eyes of the Lord, while my God was my strength, —
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
And he said, It is too light a thing that thou shouldst be my servant to raise up the tribes of Jacob, and to bring back the preserved of Israel! but I will [also] appoint thee for a light to the nations, that my salvation may reach as far as the end of the earth.
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Thus hath said the Lord, the Redeemer of Israel, his Holy One, to him who is despised by men, to him who is abhorred by nations, to the servant of rulers, Kings shall see it and rise up, princes, and they shall prostrate themselves, for the sake of the Lord, who is faithful, the Holy One of Israel, who hath made choice of thee.
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
Thus hath said the Lord, In the time of favor have I answered thee, and on the day of salvation have I helped thee; and I will preserve thee, and I will appoint thee as a people of my covenant to raise up the land, to divide out desolate heritages;
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
When I say to the prisoners, Go forth; to those that are in darkness, Show yourselves. On the roads shall they feed, and on all mountain-peaks shall be their pasture.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
They shall not be hungry nor thirsty, and neither heat nor sun shall smite them; for he that hath mercy on them will lead them, and by springs of water will he guide them.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
And I will change all my mountains into a road, and my highways shall be lifted up.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
Behold, these shall come from afar; and, lo, these from the north and from the west; and these from the land of Sinim.
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
Sing, O heavens; and be joyful, O earth; and break forth, O mountains, into song; for the Lord hath comforted his people, and upon his oppressed will he have mercy.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
Yet Zion said, the Eternal hath forsaken me, and the Lord hath forgotten me.
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
Can a woman forget her sucking child, not to have mercy on the son of her body? yea, should these even forget, yet would I not forget thee.
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
Behold, upon the palms of my hands have I engraved thee; thy walls are continually before me.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
Thy children come in haste; thy destroyers and they that laid thee waste shall go away from thee.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
Lift up thy eyes round about, and see; they all are assembled together, they come to thee: as I live, saith the Lord, thou shalt surely clothe thyself with them all, as with an ornament, and bind them on thee, as a bride.
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
For thy ruins and thy desolate places, and thy wasted land, —yea, now shall it be too narrow for thee by reason of the inhabitants, and thy destroyers shall be far away.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
Yet again will say before thy ears the children of whom thou wast deprived, The place is too narrow for me; make room for me that I may dwell.
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
And thou wilt say in thy heart, Who hath born me these, seeing I was bereft of my children, and was solitary, an exile, and outcast? and who hath brought up these? Behold, I was left entirely alone; these, where have they been?
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will lift up to the nations my hand, and to the people will I raise up high my standard; and they shall bring thy sons in [their] arms, and thy daughters shall be carried upon shoulders.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
And kings shall be thy nursing-fathers, and their princesses thy nursing-mothers; with the face toward the earth shall they bow down to thee, and the dust of thy feet shall they lick up: and thou shalt know that I am the Lord, who will not suffer those who hope in me to be ashamed.
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
Shall the prey be taken from the mighty, or shall the captive of the victor escape?
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
For thus hath said the Lord, Also the captive of the mighty shall be taken away, and the prey of the powerful shall escape; and with those who contend against thee will I contend, and thy children will I indeed save.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
And I will feed thy oppressors with their own flesh; and as with new wine shall they be made drunken with their own blood: and all flesh shall know that I the Eternal am thy Saviour, and thy Redeemer the Mighty One of Jacob.