< Yesaya 48 >
1 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo, inu amene amakutchani dzina lanu Israeli, ndinu a fuko la Yuda, inu mumalumbira mʼdzina la Yehova, ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli, ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
Poslušajte to, oh hiša Jakobova, ki ste imenovani z imenom Izrael in ste izšli iz Judovih vodá, ki prisegate pri Gospodovem imenu in omenjate Izraelovega Boga, vendar ne v resnici niti ne v pravičnosti.
2 Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Kajti imenujejo se po svetem mestu in se naslanjajo na Izraelovega Boga; Gospod nad bojevniki je njegovo ime.
3 Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale, zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza; tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Razglasil sem prejšnje stvari od začetka in izšle so iz mojih ust in pokazal sem jih; nenadoma sem jih naredil in zgodile so se.
4 Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve wa nkhongo gwaa, wa mutu wowuma.
Ker sem vedel, da si trdovratna in je tvoj vrat železna kita in tvoja obrv bron,
5 Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe; zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe kuti unganene kuti, ‘Fano langa ndilo lachita zimenezi, kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
sem ti to celo od začetka razglasil; preden se je zgodilo, sem ti to pokazal, da ne bi rekla: ›Moj malik jih je naredil, moja rezana podoba in moja ulita podoba jim je zapovedala.‹
6 Inu munamva zinthu zimenezi. Kodi inu simungazivomereze? “Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
Slišal si, videl si vse to in ali ne boš tega razglasil? Od tega časa sem ti pokazal nove stvari, celo skrite stvari in ti jih nisi poznal.
7 Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale; munali musanazimve mpaka lero lino. Choncho inu simunganene kuti, ‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
Sedaj so ustvarjene in ne od začetka; celo pred dnevom, ko jih nisi slišal, da ne bi rekel: »Glej, poznal sem jih.«
8 Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa; makutu anu sanali otsekuka. Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Da, ne slišiš; da, ne poznaš; da, od tistega časa, ko tvoje uho ni bilo odprto, kajti vedel sem, da boš postopal zelo zahrbtno in si bil od maternice imenovan prestopnik.
9 Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa. Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze. Sindidzakuwonongani kotheratu.
Zaradi svojega imena bom odložil svojo jezo in zaradi svoje hvale se bom zadržal, da te ne odsekam.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva; ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
Glej, prečistil sem te, toda ne s srebrom; izbral sem te v talilni peči stiske.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi. Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke? Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
Zaradi sebe, celó zaradi sebe, bom to storil, kajti kako bi bilo moje ime umazano? In svoje slave ne bom dal drugemu.
12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo, Israeli, amene ndinakuyitana: Mulungu uja Woyamba ndi Wotsiriza ndine.
Prisluhni mi, oh Jakob in Izrael, moj poklicani; jaz sem; jaz sem prvi, jaz sem tudi zadnji.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi, dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga. Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Moja roka je tudi položila temelj zemlji in moja desnica je razpela nebo. Ko kličem k njima, skupaj vstaneta.
14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani: Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi? Wokondedwa wa Yehova uja adzachita zomwe Iye anakonzera Babuloni; dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
Vsi vi, zberite se in poslušajte; kdo izmed njih je razglasil te stvari? Gospod ga je ljubil. Storil bo, kar mu ugaja nad Babilonom in njegov laket bo na Kaldejcih.
15 Ine, Inetu, ndayankhula; ndi kumuyitana ndidzamubweretsa ndine ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
Jaz, celó jaz, sem govoril. Da, poklical sem ga. Privedel sem ga in svojo pot bo naredil uspešno.
16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi: “Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa; pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.” Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake ndi kundituma.
Pridite blizu k meni, poslušajte to; od začetka nisem govoril na skrivnem; od časa, ko je to bilo, tam jaz sem. In sedaj me je poslal Gospod Bog in njegov Duh.«
17 Yehova, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimakuphunzitsa kuti upindule, ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
Tako govori Gospod, tvoj Odkupitelj, Sveti Izraelov: »Jaz sem Gospod, tvoj Bog, ki te učim, da boš imel koristi, ki te vodim po poti, po kateri naj bi šel.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga, bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
Oh, da bi prisluhnil mojim zapovedim! Potem bi bil tvoj mir kakor reka in tvoja pravičnost kakor morski valovi.
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga, ana ako akanachuluka ngati fumbi; dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga ndipo silikanafafanizidwa konse.”
Tudi tvojega semena bi bilo kakor peska in potomstvo tvoje notranjosti podobno njegovemu gramozu; njegovo ime ne bi bilo odrezano niti uničeno izpred mene.
20 Tulukani mʼdziko la Babuloni! Thawani dziko la Kaldeya! Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo ndipo muzilalikire mpaka kumathero a dziko lapansi; muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
Pojdite naprej iz Babilona, pobegnite od Kaldejcev, z glasom petja razglasite, povejte to, izustite to celó do konca zemlje. Recite: › Gospod je odkupil svojega služabnika Jakoba.‹
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu; anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe; anangʼamba thanthwelo ndipo munatuluka madzi.
Niso bili žejni, ko jih je vodil skozi puščave. Zanje je vodam veleval, da tečejo iz skale. Razklal je tudi skalo in iz nje so pridrle vode.
22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Tam ni miru, « govori Gospod, »zlobnemu.«