< Yesaya 48 >
1 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo, inu amene amakutchani dzina lanu Israeli, ndinu a fuko la Yuda, inu mumalumbira mʼdzina la Yehova, ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli, ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
oJanjiño zao, ry anjomba’ Iakobe, ie tokaveñe ami’ty tahina’ Israele, ry niboak’ ami’ty figoangoa’ Iehodà; o mifanta ami’ty tahina’ Iehovà naho mitalily i Andrianañahare’ Israeleo, fe tsy an-katò, tsy an-kavantañañe.
2 Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Ie manao ho mpiamy rova miavakey, naho mpiato aman’ Añahare’ Israele, Iehovà’ i Màroy ty tahina’e.
3 Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale, zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza; tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Fa nitaroñeko haehae o raha taoloo; eka fa nionjoñe boak’am-bavako ao, nitaroñeko le tsipaepae’e te nifetsake;
4 Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve wa nkhongo gwaa, wa mutu wowuma.
Amy te napotako t’ie mitangingìñe, naho viñe ty tali-bozìn-kàto’o, Vaho torisìke ty lahara’o;
5 Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe; zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe kuti unganene kuti, ‘Fano langa ndilo lachita zimenezi, kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
Aa le nivolañako boake taolo añe, ie mbe tsy nitondroke le nitaroñako, tsy mone hatao’o ty hoe; Nihenefa’ i hazomangakoy, naho i sare pinateko an-kataey, vaho, i raha natranakoy ty nandily izay.
6 Inu munamva zinthu zimenezi. Kodi inu simungazivomereze? “Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
F’ie nahajanjiñe, heheke iaby o raha zao: aa vaho tsy ho taroñe’ areo? F’ie nitaroñeko raha vao henaneo, raha mietake mbe tsy nifohi’o.
7 Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale; munali musanazimve mpaka lero lino. Choncho inu simunganene kuti, ‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
Nifonireñe henaneo, fa tsy haehae, tsy nijanjiña’o taolo’ ty andro toy, tsy mone hatao’o ty hoe t’ie nifanta’o.
8 Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa; makutu anu sanali otsekuka. Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Eka, tsy jinanji’o tsy napota’o; toe tsy nisokake o ravembia’oo haehae izay; fe napotako t’ie hikabo-draha, ihe natao mpiola boak’ an-koviñe ao.
9 Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa. Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze. Sindidzakuwonongani kotheratu.
Aa le ty añarako ty hampihankàñe o fifombokoo, i fandrengeañe ahiy ty ifoneñako, tsy mone haitoako irehe.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva; ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
Ie hinasohasoko, fa tsy hoe volafoty; nitsoheko an-toñan-kaloviloviañe ao.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi. Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke? Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
Izaho, eka izaho, ty hanao izay; fa akore te ho tivaeñe ty añarako? toe tsy hatoloko ami’ty ila’e o engekoo.
12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo, Israeli, amene ndinakuyitana: Mulungu uja Woyamba ndi Wotsiriza ndine.
Haoño iraho ry Iakobe, ry Israele kinanjiko; Izaho ro Ie, Izaho ty fifotora’e, naho Izaho ty figadoña’e.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi, dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga. Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Eka, nandaharen-tañako ty faha’ ty tane toy, nilamahen-tañako havana o likerañeo; ie tokavako, mitrao-piongake.
14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani: Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi? Wokondedwa wa Yehova uja adzachita zomwe Iye anakonzera Babuloni; dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
Mitontoña, ie iaby, vaho mijanjiña: ia am’ iereo ty nitsey o raha zao? Hanao ty satrin-arofo’e e Bavele añe t’i kokoa’ Iehovà, ie hisenge ty sira’e amo nte-Kasdio.
15 Ine, Inetu, ndayankhula; ndi kumuyitana ndidzamubweretsa ndine ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
Izaho le Izaho avao ty nivolañe, eka Izaho ty nitoka aze, Izaho ty nanese aze, Ie ty hampiraorao o lala’eo.
16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi: “Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa; pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.” Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake ndi kundituma.
Mitotoha amako le janjiño: Boak’ am-baloha’e raho tsy nivolañe añ’etake; ie vaho namoroñe le tao iraho; ie amy zao fa nañirak’ ahy naho i Arofo’ey t’Iehovà Talè
17 Yehova, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimakuphunzitsa kuti upindule, ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
Hoe t’Iehovà, Mpijebañe azo, t’i Masi’ Israele; Izaho Iehovà, Andrianañahare’o, I mpañòke azo ho ami’ty hasoa’oy, I mpiaolo azo an-dalan-kombà’oy.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga, bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
Naho ho nihaoñe’ areo o lilikoo! le ho nanahake o oñeo ty fierañeraña’o, vaho hoe onjan-driake ty havantaña’o.
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga, ana ako akanachuluka ngati fumbi; dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga ndipo silikanafafanizidwa konse.”
Le ho nira amo faseñeo o tiri’oo, o tariram-pañova’oo ami’ty hamaro’ ty haminjilita’e; naho tsy napitsoke ndra naitoañe aoloko ka ty tahina’e.
20 Tulukani mʼdziko la Babuloni! Thawani dziko la Kaldeya! Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo ndipo muzilalikire mpaka kumathero a dziko lapansi; muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
Iakaro i Bavele, Ivoratsaho o nte-Kasdio; am-peo-pisaboañe, tseizo, pazapazaho, koiho pak’ añ’olo’ ty tane toy; Ano ty hoe: Fa jineba’ Iehovà ty mpitoro’e Iakobe.
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu; anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe; anangʼamba thanthwelo ndipo munatuluka madzi.
Ie tsy nitaliñiereñe te niaoloa’e hitsake o fatram-beio; Nampipororoaha’e rano i vatoy; tsinera’e i lamilamiy vaho nidoandoañe i ranoy.
22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Po-panintsiñañe, hoe t’Iehovà, o tsivokatseo.