< Yesaya 48 >

1 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo, inu amene amakutchani dzina lanu Israeli, ndinu a fuko la Yuda, inu mumalumbira mʼdzina la Yehova, ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli, ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
E HOOLOHE oukou i keia, e ko ka hale o Iakoba, Ka poe i kapaia ma ka inoa o ka Iseraela, Ka poe hoi i laha mai, mai na wai o Iuda mai; Ka poe hoohiki ma ka inoa o Iehova, Ka poe hookaulana i ke Akua o ka Iseraela, Aole nae me ka oiaio, aole me ka pono.
2 Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
No ka mea, ua kapaia lakou mamulio ke kulanakauhale hoano, A hilinai lakou ma ke Akua o ka Iseraela, O Iehova o na kaua kona inoa.
3 Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale, zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza; tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Ua hoike aku no wau i na mea kahiko, mai kinohi mai, Mai ko'u waha i puka aku ai lakou; A na'u i hoike aku ia mau mea, Hana hoohikilele au, a hiki io mai no lakou.
4 Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve wa nkhongo gwaa, wa mutu wowuma.
No ka mea, ike mua no au, ua paakiki oe, A o kou a-i hoi, he olona hao, A o kou lae hoi, he keleawe.
5 Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe; zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe kuti unganene kuti, ‘Fano langa ndilo lachita zimenezi, kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
Nolaila, hai aku au ia oe i kela mea i kinohi; Mamau o kona hiki ana mai, hoikeike aku au ia oe, O olelo auanei oe, Na kuu kii i hana i keia mau mea, Na kuu kiikalaiia, a na kuu kiihooheheeia lakou i kauoha aku.
6 Inu munamva zinthu zimenezi. Kodi inu simungazivomereze? “Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
Ua lohe no oe, e nana hoi oe ia mea a pau; Aole anei oukou e hai aku? I keia manawa, ua hai aku au ia oe i mea hou, I na mea hoi i hunaia, na mea au i ike ole ai
7 Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale; munali musanazimve mpaka lero lino. Choncho inu simunganene kuti, ‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
I keia manawa lakou i hanaia'i, aole mai kela wa mai, I ka la hoi au i lohe ole ai ia mau mea, O olelo auanei oe, Aia, ike no wau ia.
8 Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa; makutu anu sanali otsekuka. Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Oia, aole oe i lohe, aole hoi oe i ike; Oia, mai ia manawa mai, aole i hoohakahakaia kou pepeiao; No ka mea, ike mua no wau e hana aua oe me ka hoopunipuni nui loa, A mai ka opu mai, ua kapaia hoi oe o Kipi.
9 Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa. Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze. Sindidzakuwonongani kotheratu.
No ko'u inoa no wau e hoopanee aku ai i ko'u iuaina, A no kuu nani, e hoomanawanui au ia oe, I mea e anai ole aku ai au ia oe.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva; ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
Aia hoi, ua hoohehee hoomaikai aku au ia oe, aole nae me ke kala; Ua hoao aku au ia oe ma ka umu o ka popilikia.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi. Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke? Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
No'u iho, no'u iho no wau e hana aku ai ia; No ka mea, e hoohaumiaia anei ko'u? Aole au e haawi i ko'u nani ia hai.
12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo, Israeli, amene ndinakuyitana: Mulungu uja Woyamba ndi Wotsiriza ndine.
E hoolohe mai oe ia'u, e ka Iakoba, a me ka Iseraela hoi, ko'u mea i heaia; Owau no ia, owau ka mua, owau hoi ka hope.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi, dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga. Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Oia, na ko'u lima no i hookumu i ka honua, Na kuu lima akau no i hoopalahalaha i na lani, Hea aku no au ia lakou, a ku pu mai la no lakou.
14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani: Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi? Wokondedwa wa Yehova uja adzachita zomwe Iye anakonzera Babuloni; dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
E akoakoa oukou a pau loa, a e hoolohe: Owai ka mea o lakou i hai i keia mau mea? O ka mea a Iehova i aloha aku ai, Nana no e hana kona makemake maluna o Babulona, A e kau no kona lima maluna o ko Kaledea.
15 Ine, Inetu, ndayankhula; ndi kumuyitana ndidzamubweretsa ndine ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
Owau hoi, ua olelo no owau, Oia, ua hea aku no au ia ia; A na'u hoi ia i lawe mai nei, A e hoopomaikai oia i kona hele ana.
16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi: “Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa; pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.” Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake ndi kundituma.
E hookokoke mai oukou ia'u, e hoolohe i keia; Mai kinohi mai, aole au i olelo malu, Mai kona wa i hanaia'i, malaila no au; Ano hoi, ua hoouna mai ia'u o Iehova, ka Haku, a me kona Uhane.
17 Yehova, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimakuphunzitsa kuti upindule, ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
Penei hoi ka olelo ana mai a Iehova, a kou Hoolapanai, Ka Mea Hemolele hoi o ka Iseraela; Owau no Iehova, kou Akua, Ka mea ao aku ia oe i ka mea e pono ai, Ka mea alakai ia oe ma kahi e pono ai oe ke hele.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga, bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
Ina i hoolohe mai oe i ka'u mau kauoha, Ina ua like kou malu me ka muliwai, A o kou pono hoi, me na aui o ka moana:
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga, ana ako akanachuluka ngati fumbi; dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga ndipo silikanafafanizidwa konse.”
Ina ua like kau poe mamo me ke one, A me na keiki o kou opu me kona iliili; Aole hoi e hookiia kona inoa, aole hoi e hookaia'ku imua o'u.
20 Tulukani mʼdziko la Babuloni! Thawani dziko la Kaldeya! Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo ndipo muzilalikire mpaka kumathero a dziko lapansi; muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
O haele oukou mawaho o Babulona, E holo oukou, mai ko Kaledea aku, Me ka leo o ke oli, e hai aku, e hookaulana i keia, E hoolaha aku a i na kukulu o ka honua; E i aku, Ua hoolapanai o Iehova i ka Iakoba, kana kauwa.
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu; anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe; anangʼamba thanthwelo ndipo munatuluka madzi.
Ia lakou i hele ai ma na wahi maloo, aole lakou i make wai: Hookahe oia i ka wai, mai loko mai o ka pohaku no lakou; Wawahi no oia i ka pohaku, a huai mai la na wai.
22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Aole malu no ka poe hewa, wahi a Iehova.

< Yesaya 48 >