< Yesaya 47 >

1 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi, iwe namwali, Babuloni; khala pansi wopanda mpando waufumu, iwe namwali, Kaldeya pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera kumugwira mosamala.
Кобоарэ-те ши шезь ын цэрынэ, фечоарэ, фийка Бабилонулуй; шезь пе пэмынт, фэрэ скаун де домние, фийка халдеенилор, кэч ну те вор май нуми субцирикэ ши плэкутэ.
2 Tenga mphero ndipo upere ufa; chotsa nsalu yako yophimba nkhope kwinya chovala chako mpaka ntchafu ndipo woloka mitsinje.
Я петреле де моарэ ши мачинэ фэинэ; скоате-ць марама, ридикэ-ць поала рокией, дескоперэ-ць пичоареле, тречь рыуриле!
3 Maliseche ako adzakhala poyera ndipo udzachita manyazi. Ndidzabwezera chilango ndipo palibe amene adzandiletse.”
Голичуня ци се ва дескопери ши ци се ва ведя рушиня. Мэ вой рэзбуна ши ну вой круца пе нимень.”
4 Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Рэскумпэрэторул ностру Се кямэ Домнул оштирилор, Сфынтул луй Исраел.
5 “Khala chete, ndipo lowa mu mdima, iwe namwali, Kaldeya; chifukwa sadzakutchulanso mfumukazi ya maufumu.
„Шезь ынтр-ун колц ши тачь, фата халдеенилор, кэч ну те вор май нуми ымпэрэтяса ымпэрэциилор.
6 Ndinawakwiyira anthu anga, osawasamalanso. Ndinawapereka manja mwako, ndipo iwe sunawachitire chifundo. Iwe unachitira nkhanza ngakhale nkhalamba.
Мэ мыниясем пе попорул Меу, Ымь пынгэрисем моштениря ши-й дэдусем ын мыниле тале, дар ту н-ай авут милэ де ей, чи ць-ай апэсат греу жугул асупра бэтрынулуй.
7 Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse ngati mfumukazi.’ Koma sunaganizire zinthu izi kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
Ту зичяй: ‘Ын вечь вой фи ымпэрэтясэ!’ ши ну те-ай гындит, нич н-ай висат кэ лукрул ачеста аре сэ се сфыршяскэ.
8 “Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe, amene ukukhala mosatekesekawe, umaganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina. Sindidzakhala konse mkazi wamasiye, ndipo ana anga sadzamwalira.’
Аскултэ ынсэ акум, ту, чя дедатэ плэчерилор, каре стай фэрэ грижэ ши зичь ын инима та: ‘Еу, ши нумай еу, ну вой фи ничодатэ вэдувэ ши ну вой фи ничодатэ липситэ де копий!’
9 Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi, zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira: ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye. Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu ngakhale ali ndi amatsenga ambiri ndi mawula amphamvu.
Ши тотушь ачесте доуэ лукрурь ци се вор ынтымпла деодатэ, ын ачеяшь зи: ши пердеря копиилор, ши вэдувия; вор кэдя асупра та ку путере маре, ын чуда тутурор врэжиториилор тале ши мултелор тале дескынтече.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’ Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza, choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
Кэч те ынкредяй ын рэутатя та ши зичяй: ‘Нимень ну мэ веде!’ Ынцелепчуня ши штиинца та те-ау амэӂит, де зичяй ын инима та: ‘Еу ши нумай еу.’
11 Ngozi yayikulu idzakugwera ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako. Mavuto adzakugwera ndipo sudzatha kuwachotsa; chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa chidzakugwera mwadzidzidzi.
Де ачея ненорочиря ва вени песте тине фэрэ сэ-й везь зориле; урӂия ва кэдя песте тине фэрэ с-о поць ымпэка ши деодатэ ва вени песте тине прэпэдул, пе неаштептате.
12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako, pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo, wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako. Mwina udzatha kupambana kapena kuopsezera nazo adani ako.
Вино дар ку дескынтечеле тале ши ку мулцимя врэжиториилор тале, кэрора ць-ай ынкинат мунка дин тинереце; поате кэ вей путя сэ траӂь вреун фолос дин еле, поате кэ вей избути.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi! Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni. Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi zimene ziti zidzakuchitikire.
Те-ай обосит тот ынтребынд: сэ се скоале дар ши сэ те скапе чей че ымпарт черул, каре пындеск стелеле, каре вестеск, дупэ луниле ной, че аре сэ ци се ынтымпле!
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi; adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa okha ku mphamvu ya malawi a moto. Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha; kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
Ятэ-й, ау ажунс ка мириштя пе каре о арде фокул ши ну-шь вор скэпа вяца дин флэкэрь, кэч ну ва фи ка ун кэрбуне ла каре се ынкэлзеште чинева, нич ка ун фок ла каре стэ.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga, anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako. Onse adzamwazika ndi mantha, sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
Аша ва фи соарта ачелора пе каре те обосяй сэ-й ынтребь. Ши чей ку каре ай фэкут негоц дин тинереця та се вор рисипи фиекаре ынтр-о парте ши ну ва фи нимень каре сэ-ць винэ ын ажутор.

< Yesaya 47 >