< Yesaya 47 >

1 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi, iwe namwali, Babuloni; khala pansi wopanda mpando waufumu, iwe namwali, Kaldeya pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera kumugwira mosamala.
Yehla, uhlale othulini, ntombi emsulwa, ndodakazi yeBhabhiloni; hlala emhlabathini; akulasihlalo sobukhosi, ndodakazi yamaKhaladiya; ngoba kawusayikubizwa ngokuthi uthambile njalo ubuthakathaka.
2 Tenga mphero ndipo upere ufa; chotsa nsalu yako yophimba nkhope kwinya chovala chako mpaka ntchafu ndipo woloka mitsinje.
Thatha amatshe okuchola, uchole impuphu, wembule isimbombozo sakho, ukhwince ilogwe, uveze umlenze, uchaphe imifula.
3 Maliseche ako adzakhala poyera ndipo udzachita manyazi. Ndidzabwezera chilango ndipo palibe amene adzandiletse.”
Ubunqunu bakho buzakwembulwa, yebo, ihlazo lakho libonakale. Ngizaphindisela, ngingahlangani lawe njengomuntu.
4 Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
UMhlengi wethu, iNkosi yamabandla libizo lakhe, oyiNgcwele kaIsrayeli.
5 “Khala chete, ndipo lowa mu mdima, iwe namwali, Kaldeya; chifukwa sadzakutchulanso mfumukazi ya maufumu.
Hlala ngokuthula, ungene emnyameni, ndodakazi yamaKhaladiya; ngoba kawusayikubizwa ngokuthi: Nkosikazi yemibuso.
6 Ndinawakwiyira anthu anga, osawasamalanso. Ndinawapereka manja mwako, ndipo iwe sunawachitire chifundo. Iwe unachitira nkhanza ngakhale nkhalamba.
Ngabathukuthelela abantu bami, ngangcolisa ilifa lami, ngabanikela esandleni sakho; kawubenzelanga izihawu; walenza laba nzima kakhulu ijogwe lakho phezu komdala.
7 Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse ngati mfumukazi.’ Koma sunaganizire zinthu izi kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
Wena wathi: Ngizakuba yinkosikazi njalonjalo; kawukabeki lezizinto enhliziyweni yakho, kawukhumbulanga isiphetho sakho.
8 “Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe, amene ukukhala mosatekesekawe, umaganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina. Sindidzakhala konse mkazi wamasiye, ndipo ana anga sadzamwalira.’
Khathesi-ke zwana lokhu, wena ozithokozisayo, ohlezi uvikelekile, othi enhliziyweni yakho: Yimi, njalo kakho omunye ngaphandle kwami; kangiyikuhlala okomfelokazi, kangiyikwazi ukufelwa ngabantwana.
9 Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi, zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira: ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye. Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu ngakhale ali ndi amatsenga ambiri ndi mawula amphamvu.
Kodwa lezizinto ezimbili zizakwehlela ngokucwayiza kwelihlo ngasuku lunye: Ukufelwa ngabantwana lobufelokazi; kuzakwehlela phezu kwakho ngokuphelela kwakho, ngenxa yobunengi bobuthakathi bakho, ngenxa yobunengi obukhulu bamalumbo akho.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’ Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza, choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
Ngoba wathembela ebubini bakho, wathi: Kakho ongibonayo. Inhlakanipho yakho lolwazi lwakho khona kwakuphambula, wathi enhliziyweni yakho: Yimi, njalo kakho omunye ngaphandle kwami.
11 Ngozi yayikulu idzakugwera ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako. Mavuto adzakugwera ndipo sudzatha kuwachotsa; chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa chidzakugwera mwadzidzidzi.
Ngakho ububi buzakwehlela, kawusoze wazi lapho obenyuka khona; lengozi izakwehlela, ongelakho ukwenza inhlawulo yokuthula ngayo; lencithakalo ihle yehlele phezu kwakho, ungazi.
12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako, pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo, wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako. Mwina udzatha kupambana kapena kuopsezera nazo adani ako.
Mana khathesi ngamalumbo akho langobunengi bobuthakathi bakho otshikatshike kukho kusukela ebutsheni bakho; mhlawumbe uzakuba lakho ukuba lenzuzo, mhlawumbe unqobe.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi! Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni. Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi zimene ziti zidzakuchitikire.
Udiniwe ebunengini bamacebo akho; kakuthi basukume khathesi abahloli bamazulu, abakhangela izinkanyezi, abazisa ngezinyanga, bakusindise kwezizakwehlela.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi; adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa okha ku mphamvu ya malawi a moto. Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha; kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
Khangela, bazakuba njengamabibi; umlilo uzabatshisa; kabayikuzophula emandleni elangabi; lingabikho ilahle lokotha, umlilo wokuhlala phambi kwawo.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga, anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako. Onse adzamwazika ndi mantha, sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
Bazakuba njalo kuwe labo owatshikatshika labo, owathengiselana labo kusukela ebutsheni bakho; bazazulazula, ngulowo lalowo ngendlela yakhe; kakuyikuba lomsindisi wakho.

< Yesaya 47 >