< Yesaya 46 >
1 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Bel se inclina. Nebo se inclina. Sus ídolos son llevados por animales, y en el ganado. Las cosas que llevabas son cargas pesadas, una carga para los cansados.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
Se agachan y se inclinan juntos. No pudieron entregar la carga, pero han ido al cautiverio.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
“Escúchame, casa de Jacob, y todo el resto de la casa de Israel, que llevan desde su nacimiento, que se han llevado desde el vientre materno.
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
Hasta la vejez soy yo, y hasta las canas te llevaré. He hecho, y soportaré. Sí, llevaré y entregaré.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
“¿Con quién me compararás y me considerarás igual? y compararme, como si fuéramos iguales?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
Algunos vierten oro de la bolsa, y pesa la plata en la balanza. Contratan a un orfebre, y lo convierte en un dios. Se caen... sí, adoran.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
Lo llevan al hombro. Lo llevan y lo colocan en su sitio, y allí se queda. No puede moverse de su sitio. Sí, se le puede gritar, pero no puede responder. No puede salvarle de su problema.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
“Recordad esto y mostraos como hombres. Recuérdenlo, transgresores.
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
Acuérdate de las cosas antiguas; porque yo soy Dios y no hay otro. Yo soy Dios, y no hay nadie como yo.
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
Declaro el fin desde el principio, y de los tiempos antiguos las cosas que aún no se han hecho. Yo digo: Mi consejo se mantendrá, y haré todo lo que me plazca.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
Llamo a un pájaro voraz del este, el hombre de mi consejo desde un país lejano. Sí, he hablado. Yo también lo llevaré a cabo. Lo he planeado. Yo también lo haré.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
Escúchame, terco de corazón, ¡que están lejos de la justicia!
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
Acerco mi justicia. No está lejos, y mi salvación no esperará. Yo concederé la salvación a Sión, mi gloria a Israel.