< Yesaya 46 >
1 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Bel bows down, Nebo stoops; their idols are carried by animals and beasts of burden. These idols that you carry are a heavy burden for weary animals.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
Together they bend low, kneel down; they cannot rescue the images, and they themselves have gone off into captivity.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
Listen to me, house of Jacob, all the remnant of the house of Israel, who have been carried by me from before your birth, carried from the womb.
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
Even to your old age I am he, and until your hair is gray I will carry you. I made you and I will bear you; I will carry you and I will rescue you.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
To whom will you compare me? Who do you think I resemble, so that we may be compared?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
People pour out gold from the bag and weigh silver on the scale. They hire a metalsmith, and he makes it into a god; they bow down and worship it.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
They lift it on their shoulder and carry it; they set it in its place, and it stands in its place and does not move from it. They cry out to it, but it cannot answer nor save anyone from his trouble.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
Think about these things; never ignore them, you rebels!
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
Think about the earlier things, those of times past, for I am God, and there is no other, I am God, and there is no one like me.
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
I announce the end from the beginning, and beforehand what has not yet happened; I say, “My plan will happen, and I will do as I desire.”
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
I call a bird of prey from the east, the man of my choice from a distant land; yes, I have spoken; I will also accomplish it; I have purposed, I will also do it.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
Listen to me, you stubborn people, who are far from doing what is right.
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
I am bringing my righteousness near; it is not far away, and my salvation does not wait; and I will give salvation to Zion and my beauty to Israel.