< Yesaya 45 >

1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
Ovako govori Gospod pomazaniku svojemu Kiru, kojega držim za desnicu, da oborim pred njim narode i careve raspašem, da se otvoraju vrata pred njim i da ne budu vrata zatvorena:
2 Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
Ja æu iæi pred tobom, i putove neravne poravniæu, vrata mjedena razbiæu i prijevornice gvozdene slomiæu.
3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
I daæu ti blago tajno i bogatstvo sakriveno, da poznaš da sam ja Gospod Bog Izrailjev, koji te zovem po imenu.
4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
Radi sluge svojega Jakova i Izrailja izbranika svojega prozvah te imenom tvojim i prezimenom, premda me ne znaš.
5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
Ja sam Gospod, i nema drugoga, osim mene nema boga; opasah te, premda me ne znaš,
6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
Da bi poznali od istoka sunèanoga i od zapada da nema drugoga osim mene; ja sam Gospod i nema drugoga,
7 Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
Koji pravim svjetlost i stvaram mrak, gradim mir i stvaram zlo; ja Gospod èinim sve to.
8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
Rosite, nebesa, ozgo, i oblaci neka kaplju pravdom, neka se otvori zemlja i neka rodi spasenjem i zajedno neka uzraste pravda; ja Gospod stvorih to.
9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
Teško onom ko se svaða s tvorcem svojim; crijep s drugim crepovima neka se svaða; ali hoæe li kao reæi lonèaru svojemu: šta radiš? za tvoj posao nema ruku.
10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
Teško onom ko govori ocu: što raðaš? i ženi: što se poraðaš?
11 “Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
Ovako veli Gospod svetac Izrailjev i tvorac njegov: pitajte me što æe biti; za sinove moje i za djelo ruku mojih nareðujte mi.
12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
Ja sam naèinio zemlju i èovjeka na njoj stvorio, ja sam razapeo nebesa svojim rukama, i svoj vojsci njihovoj dao zapovijest.
13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
Ja ga podigoh u pravdi, i sve putove njegove poravniæu; on æe sazidati moj grad i roblje moje otpustiæe, ne za novce ni za darove, veli Gospod nad vojskama.
14 Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
Ovako veli Gospod: trud Misirski i trgovina Etiopska i Savaca ljudi visoka rasta doæi æe k tebi i biti tvoja; za tobom æe pristati, u okovima æe iæi, i tebi æe se klanjati, tebi æe se moliti govoreæi: doista, Bog je u tebi, i nema drugoga Boga.
15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
Da, ti si Bog, koji se kriješ, Bog Izrailjev, spasitelj.
16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
Oni æe se svi postidjeti i posramiti, otiæi æe sa sramotom svikoliki koji grade likove.
17 Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
A Izrailja æe spasti Gospod spasenjem vjeènijem, neæete se postidjeti niti æete se osramotiti dovijeka.
18 Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
Jer ovako veli Gospod, koji je stvorio nebo, Bog, koji je sazdao zemlju i naèinio je i utvrdio, i nije je stvorio naprazno, nego je naèinio da se na njoj nastava: ja sam Gospod, i nema drugoga.
19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
Nijesam govorio tajno ni na mraènu mjestu na zemlji, nijesam rekao sjemenu Jakovljevu: tražite me uzalud. Ja Gospod govorim pravdu, javljam što je pravo.
20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
Skupite se i doðite, pristupite svi koji ste se izbavili izmeðu naroda. Ništa ne znaju koji nose drvo od svojega lika i mole se bogu koji ne može pomoæi.
21 Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
Oglasite, i dovedite, neka vijeæaju zajedno: ko je to od starine kazao? ko je javio još onda? Nijesam li ja, Gospod? Nema osim mene drugoga Boga, nema Boga pravednoga i spasitelja drugoga osim mene.
22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
Pogledajte u mene, i spašæete se svi krajevi zemaljski; jer sam ja Bog, i nema drugoga.
23 Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
Sobom se zakleh; izide iz usta mojih rijeè pravedna, i neæe se poreæi, da æe mi se pokloniti svako koljeno, i zaklinjati se svaki jezik,
24 Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
I govoriæe: u Gospodu je pravda i sila; k njemu æe doæi; ali æe se posramiti svi koji se gnjeve na nj.
25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
U Gospodu æe se opravdati i proslaviti sve sjeme Izrailjevo.

< Yesaya 45 >