< Yesaya 45 >
1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
Ainsi parle Yahweh à son oint, à Cyrus, que j’ai pris par la main droite pour terrasser devant lui les nations, et pour délier la ceinture des rois, pour ouvrir devant lui les portes, afin que les entrées ne lui soient pas fermées:
2 Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
Moi, je marcherai devant toi; j’aplanirai les chemins montueux; je romprai les portes d’airain, et je briserai les verrous de fer.
3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
Je te donnerai les trésors cachés, et les richesses enfouies, afin que tu saches que je suis Yahweh, le Dieu d’Israël, qui t’ai appelé par ton nom.
4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
A cause de Jacob, mon serviteur, et d’Israël, mon élu, je t’ai appelé par ton nom; je t’ai désigné quand tu ne me connaissais pas.
5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
Je suis Yahweh, et il n’y en a pas d’autre; hors moi, il n’y a pas de Dieu! Je t’ai ceint quand tu ne me connaissais pas,
6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
afin que l’on sache, du levant au couchant, qu’il n’y a rien en dehors de moi! Je suis Yahweh, et il n’y en a pas d’autre;
7 Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
je forme la lumière et crée les ténèbres, je fais la paix et je crée le malheur: c’est moi Yahweh qui fais tout cela.
8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
Cieux, répandez d’en haut votre rosée, et que les nuées fassent pleuvoir la justice! Que la terre s’ouvre et produise le salut, qu’elle fasse germer la justice en même temps! Moi! Yahweh, je crée ces choses.
9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
Malheur à qui conteste avec celui qui l’a formé, vase parmi des vases de terre! L’argile dira-t-elle à celui qui la façonne: « Que fais-tu? » Ton œuvre dira-t-elle: « Il n’a pas de mains? »
10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
Malheur à qui dit à un père: « Pourquoi engendres-tu? » Et à une femme: « Pourquoi mets-tu au monde? »
11 “Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
Ainsi parle Yahweh, le Saint d’Israël et celui qui l’a formé: « Oserez-vous m’interroger sur l’avenir, me commander au sujet de mes enfants et de l’œuvre de mes mains?
12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
C’est moi qui ai fait la terre, et qui sur elle ai créé l’homme; c’est moi dont les mains ont déployé les cieux, moi qui commande à toute leur armée.
13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
C’est moi qui l’ai suscité dans ma justice, et j’aplanis toutes ses voies. C’est lui qui rebâtira ma ville, et renverra mes captifs, sans rançon ni présents, dit Yahweh des armées.
14 Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
Ainsi parle Yahweh: Les gains de l’Égypte et les profits de l’Ethiopie, et les Sabéens à la haute stature viendront à toi et seront à toi, ils marcheront à ta suite; ils passeront enchaînés, et se prosterneront devant toi; ils te diront en suppliant: « Il n’y a de Dieu que chez toi, et il n’y en a pas d’autre, nul autre Dieu absolument! »
15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
En vérité, vous êtes un Dieu caché, Dieu d’Israël, ô Sauveur!
16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
Ils sont tous honteux et confus, ils s’en vont confus, les fabricateurs d’idoles.
17 Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
Israël est sauvé par Yahweh d’un salut éternel; vous n’aurez ni honte ni confusion dans les siècles à venir.
18 Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
Car ainsi parle Yahweh, qui a créé les cieux, lui, le Dieu qui a formé la terre, qui l’a achevée et affermie, qui n’en a pas fait un chaos, mais l’a formée pour être habitée: Je suis Yahweh, et il n’y en a pas d’autre!
19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
Je n’ai pas parlé en cachette, dans un lieu obscur de la terre. Je n’ai pas dit à la race de Jacob: « Cherchez-moi vainement! » Moi, Yahweh, je dis ce qui est juste, j’annonce la vérité.
20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
Assemblez-vous et venez; approchez ensemble, réchappés des nations. Ils ne savent rien, ceux qui portent leur idole de bois, et invoquent un dieu qui ne sauve pas.
21 Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
Appelez-les, faites-les approcher, et qu’ils se consultent ensemble! Qui a fait entendre ces choses dès le commencement, et depuis longtemps les a annoncées? N’est-ce pas moi, Yahweh? Et il n’y a pas de Dieu en dehors de moi; Moi, le Dieu juste, et il n’y a pas d’autre sauveur que moi.
22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
Tournez-vous vers moi, et vous serez sauvés, vous tous habitants de la terre, car je suis Dieu, et il n’y en a pas d’autre.
23 Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
Je l’ai juré par moi-même; de ma bouche sort la vérité, une parole qui ne sera pas révoquée: Tout genou fléchira devant moi, Et toute langue me prêtera serment.
24 Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
« En Yahweh seul, dira-t-on de moi, résident la justice et la force! » On viendra à lui; mais ils seront confondus, tous ceux qui étaient enflammés contre lui.
25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
En Yahweh sera justifiée et sera glorifiée toute la race d’Israël.