< Yesaya 45 >

1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
thus to say LORD to/for anointed his to/for Cyrus which to strengthen: hold in/on/with right his to/for to subdue to/for face: before his nation and loin king to open to/for to open to/for face: before his door and gate not to shut
2 Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
I to/for face: before your to go: went and to honor (to smooth *Q(K)*) door bronze to break and bar iron to cut down/off
3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
and to give: give to/for you treasure darkness and treasure hiding because to know for I LORD [the] to call: call to in/on/with name your God Israel
4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
because servant/slave my Jacob and Israel chosen my and to call: call to to/for you in/on/with name your to flatter you and not to know me
5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
I LORD and nothing still exception me nothing God to gird you and not to know me
6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
because to know from east sun (and from west her *LAH(b)*) for end beside me I LORD and nothing still
7 Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
to form: formed light and to create darkness to make peace: well-being and to create bad: evil I LORD to make: do all these
8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
to drip heaven from above and cloud to flow righteousness to open land: country/planet and be fruitful salvation and righteousness to spring unitedness I LORD to create him
9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
woe! to contend with to form: formed him earthenware with earthenware land: soil to say clay to/for to form: formed him what? to make and work your nothing hand to/for him
10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
woe! to say to/for father what? to beget and to/for woman what? to twist: writh in pain [emph?]
11 “Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
thus to say LORD holy Israel and to form: formed him [the] to come to ask me upon son: child my and upon work hand my to command me
12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
I to make land: country/planet and man upon her to create I hand my to stretch heaven and all army their to command
13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
I to rouse him in/on/with righteousness and all way: conduct his to smooth he/she/it to build city my and captivity my to send: let go not in/on/with price and not in/on/with bribe to say LORD Hosts
14 Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
thus to say LORD toil Egypt and profit Cush and Sabeans human measure upon you to pass and to/for you to be after you to go: follow in/on/with fetter to pass and to(wards) you to bow to(wards) you to pray surely in/on/with you God and nothing still end God
15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
surely you(m. s.) God to hide God Israel to save
16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
be ashamed and also be humiliated all their together to go: went in/on/with shame artificer image
17 Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
Israel to save in/on/with LORD deliverance: salvation forever: enduring not be ashamed and not be humiliated till forever: enduring perpetuity
18 Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
for thus to say LORD to create [the] heaven he/she/it [the] God to form: formed [the] land: country/planet and to make her he/she/it to establish: make her not formlessness to create her to/for to dwell to form: formed her I LORD and nothing still
19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
not in/on/with secrecy to speak: speak in/on/with place land: country/planet darkness not to say to/for seed: children Jacob formlessness to seek me I LORD to speak: speak righteousness to tell uprightness
20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
to gather and to come (in): come to approach: approach together survivor [the] nation not to know [the] to lift: bear [obj] tree: wood idol their and to pray to(wards) god not to save
21 Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
to tell and to approach: bring also to advise together who? to hear: proclaim this from front: old from the past to tell her not I LORD and nothing still God from beside me God righteous and to save nothing exception me
22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
to turn to(wards) me and to save all end land: country/planet for I God and nothing still
23 Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
in/on/with me to swear to come out: come from lip my righteousness word and not to return: return for to/for me to bow all knee to swear all tongue
24 Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
surely in/on/with LORD to/for me to say righteousness and strength till him to come (in): come and be ashamed all [the] to be incensed in/on/with him
25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
in/on/with LORD to justify and to boast: boast all seed: children Israel

< Yesaya 45 >