< Yesaya 45 >

1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
Thus he says Yahweh to anointed his to Cyrus whom I have taken hold on right [hand] his to subdue before him nations and [the] loins of kings I will loosen to open before him doors and gates not they will be shut.
2 Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
I before you I will go and [the] mountainous land (I will make smooth *Q(K)*) doors of bronze I will break and bars of iron I will cut through.
3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
And I will give to you treasures of darkness and hidden treasures of secret places so that you may know that I [am] Yahweh who calls by name your [the] God of Israel.
4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
For [the] sake of servant my Jacob and Israel chosen one my and I summoned you by name your I will give a title you and not you know me.
5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
I [am] Yahweh and there not [is] yet besides me there not [is] a god I will gird you and not you know me.
6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
So that they may know from [the] rising of [the] sun (and from setting place its *LAH(b)*) that nothing [is] apart from me I [am] Yahweh and there not [is] yet.
7 Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
[who] forms Light and [who] creates darkness [who] brings about well-being and [who] creates calamity I [am] Yahweh [who] does all these [things].
8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
Drip down O heaven above and clouds let them flow righteousness let it open up [the] earth so they may bear fruit salvation and righteousness let it cause to sprout together I Yahweh I have created it.
9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
Woe to! [one who] contends with [the one who] formed him a potsherd with potsherds of [the] ground ¿ does it say clay to [the one who] forms it what? are you making and work your not hands [belong] to him.
10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
Woe to! [one who] says to a father what? are you fathering and to a woman what? are you in labor with!
11 “Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
Thus he says Yahweh [the] holy [one] of Israel and [the] [one who] formed it the coming [things] ask me on children my and on [the] work of hands my you command me.
12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
I I made [the] earth and humankind on it I created I hands my they stretched out [the] heavens and all host their I commanded.
13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
I I have stirred up him in righteousness and all ways his I will make smooth he he will build city my and exile[s] my he will let go not for hire and not for a bribe he says Yahweh of hosts.
14 Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
Thus - he says Yahweh [the] produce of Egypt and [the] traffic of Cush and [the] Sabeans people of stature to you they will pass over and to you they will belong behind you they will walk in fetters they will pass over and to you they will bow down to you they will pray surely [is] among you God and there not [is] yet there not [are] gods.
15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
Truly you [are] a God [who] hides himself O God of Israel deliverer.
16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
They will be ashamed and also they will be put to shame all of them alike they will walk in ignominy craftsmen of images.
17 Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
Israel it has been saved by Yahweh a salvation of everlastingness not you will be ashamed and not you will be put to shame until everlastingness of perpetuity.
18 Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
For thus he says Yahweh [who] created the heavens he [is] God [who] formed the earth and [who] made it he he established it not a wasteland he created it to dwell in he formed it I [am] Yahweh and there not [is] yet.
19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
Not in secrecy I spoke in a place of a land of darkness not I said to [the] offspring of Jacob emptiness seek me I Yahweh [am] speaking righteousness [I am] declaring uprightness.
20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
Gather together and come draw near together O fugitives of the nations not they know those [who] carry [the] wood of idol their and [those who] pray to a god [which] not it will save.
21 Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
Declare and bring near also let them take counsel together who? did he proclaim this from antiquity from then did he declare? it ¿ not [was it] I Yahweh and there not again [is] a god except me [is] a God righteous and a deliverer there not besides me.
22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
Turn to me and be saved O all [the] ends of [the] earth for I [am] God and there not [is] yet.
23 Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
By myself I swear it goes forth from mouth my righteousness a word and not it will return that to me it will bow down every knee it will swear every tongue.
24 Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
Only [are] in Yahweh of me anyone will say righteousness and strength to him everyone will go and they may be ashamed all those [who] are angry with him.
25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
By Yahweh they will be justified and they may boast all [the] offspring of Israel.

< Yesaya 45 >