< Yesaya 45 >

1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
Thus saith the Lord God to my anointed Cyrus, whose right hand I have held, that nations might be obedient before him; and I will break through the strength of kings; I will open doors before him, and cities shall not be closed.
2 Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
I will go before thee, and will level mountains: I will break to pieces brazen doors, and burst iron bars.
3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
And I will give thee the treasures of darkness, I will open to thee hidden, unseen [treasures], that thou mayest know that I, the Lord thy God, that call thee by name, am the God of Israel.
4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
For the sake of my servant Jacob, and Israel mine elect, I will call thee by thy name, and accept thee: but thou hast not known me.
5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
For I am the Lord God, and there is no other God beside me; I strengthened thee, and thou hast not known me.
6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
That they that [come] from the east and they that [come] from the west may know that there is no God but me. I am the Lord God, and there is none beside.
7 Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
I am he that prepared light, and formed darkness; who make peace, and create evil; I am the Lord God, that does all these things.
8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
Let the heaven rejoice from above, and let the clouds rain righteousness: let the earth bring forth, and blossom [with] mercy, and bring forth righteousness likewise: I am the Lord that created thee.
9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
What excellent thing have I prepared as clay of the potter? Will the ploughman plough the earth all day? shall the clay say to the potter, What art thou doing that thou dost not work, nor hast hands? shall the thing formed answer him that formed it?
10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
As though one should say to [his] father, What wilt thou beget me? and to his mother, What art thou bringing forth?
11 “Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
For thus saith the Lord God, the Holy One of Israel, who has formed the things that are to come, Enquire of me concerning my sons, and concerning the works of my hands command me.
12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
I have made the earth, and man upon it: I with my hand have established the heaven; I have given commandment to all the stars.
13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
I have raised him up [to be] a king with righteousness, and all his ways are right: he shall build my city, and shall turn the captivity of my people, not for ransoms, nor for rewards, saith the Lord of hosts.
14 Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
Thus saith the Lord of hosts, Egypt has laboured [for thee]; and the merchandise of the Ethiopians, and the Sabeans, men of stature, shall pass over to thee, and shall be thy servants; and they shall follow after thee bound in fetters, and shall pass over to thee, and shall do obeisance to thee, and make supplication to thee: because God is in thee; and there is no God beside thee, [O Lord].
15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
For thou art God, yet we knew [it] not, the God of Israel, the Saviour.
16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
All that are opposed to him shall be ashamed and confounded, and shall walk in shame: ye isles, keep a feast to me.
17 Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
Israel is saved by the Lord with an everlasting salvation: they shall not be ashamed nor confounded for evermore.
18 Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
Thus saith the Lord that made the heaven, this God that created the earth, and made it; he marked it out, he made it not in vain, but formed it to be inhabited: I am the Lord, and there is none beside.
19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
I have not spoken in secret, nor in a dark place of the earth: I said not to the seed of Jacob, Seek vanity: I, even I, am the Lord, speaking righteousness, and proclaiming truth.
20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
Assemble yourselves and come; take counsel together, ye that escape of the nations: they that set up wood, [even] their graven image, have no knowledge, nor they who pray to gods that do not save.
21 Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
If they will declare, let them draw nigh, that they may know together, who has caused these things to be heard from the beginning: then was it told you. I am God, and there is not another beside me; a just [God] and a Saviour; there is none but me.
22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
Turn ye to me, and ye shall be saved, ye that [come] from the end of the earth: I am God, and there is none other.
23 Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
By myself I swear, righteousness shall surely proceed out of my mouth; my words shall not be frustrated; that to me every knee shall bend, and every tongue shall swear by God,
24 Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
saying, Righteousness and glory shall come to him: and all that remove them from their borders shall be ashamed.
25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
By the Lord shall they be justified, and in God shall all the seed of the children of Israel be glorified.

< Yesaya 45 >