< Yesaya 44 >
1 Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
A teraz słuchaj, Jakubie, mój sługo, i ty, Izraelu, którego wybrałem.
2 Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
Tak mówi PAN, który cię uczynił i który cię ukształtował już od łona matki, i który cię wspomaga: Nie bój się, Jakubie, mój sługo, i Jeszurunie, którego wybrałem.
3 Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
Wyleję bowiem wody na spragnionego, a potoki na suchą ziemię. Wyleję mego Ducha na twoje potomstwo i moje błogosławieństwo na twoich potomków.
4 Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
I rozkrzewią się tak jakby pomiędzy trawą i jak wierzby nad potokami wód.
5 Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
Jeden powie: Ja należę do PANA, drugi nazwie się imieniem Jakuba, a inny napisze swoją ręką: PANU, i będzie się nazywał imieniem Izraela.
6 “Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
Tak mówi PAN, Król Izraela i jego Odkupiciel, PAN zastępów: Ja jestem pierwszy i ja jestem ostatni, a oprócz mnie nie ma Boga.
7 Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
Czy od czasów, gdy ustanowiłem pierwszy lud na świecie, znalazł się ktoś, kto jak ja jest w stanie ogłosić i opowiedzieć rzeczy przyszłe? Jeśli tak – niech więc powie, co ma nastąpić.
8 Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
Nie bójcie się i nie lękajcie. Czy od dawna nie oznajmiałem wam [wszystkiego] i nie opowiadałem? Wy sami jesteście moimi świadkami. Czy jest Bóg oprócz mnie? Nie ma innej Skały; nie znam żadnej.
9 Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
Wytwórcy rzeźbionych posągów są niczym, a ich piękne dzieła nic im nie pomogą; oni sami sobie są świadkami, że nic nie widzą ani nie rozumieją – ku swemu zawstydzeniu.
10 Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
Kto utworzył boga i odlewał posąg, który nie przynosi żadnego pożytku?
11 Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
Oto wszyscy jego towarzysze będą zawstydzeni. Rzemieślnicy są tylko ludźmi. Niech się zbiorą wszyscy i niech staną. Przelęknąć się muszą i razem będą zawstydzeni.
12 Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
Kowal kleszczami pracuje przy węglu, młotami kształtuje posąg i wykonuje go siłą swoich ramion, aż z głodu jego siły opadają, wody nie pije i omdlewa.
13 Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
Cieśla zaś rozciąga sznur, wyznacza farbowanym sznurem, ciosa toporem, zaznacza go cyrklem i wykonuje go na podobieństwo człowieka, na podobieństwo pięknego człowieka, aby pozostawał w domu.
14 Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
Narąbie sobie cedrów i bierze cyprys i dąb lub to, co jest najsilniejsze spośród drzew leśnych, wsadzi jesion, który rośnie dzięki deszczom.
15 Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
Wtedy służy to człowiekowi na opał: bierze z tego, aby się ogrzać, także roznieca ogień, aby upiec chleb, ponadto robi sobie boga i oddaje mu pokłon, czyni z tego posąg i pada przed nim.
16 Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
Część tego spala w ogniu, przy drugiej części je mięso – przyrządza pieczeń i syci się. Także grzeje się i mówi: Ach, jak mi ciepło, widziałem ogień.
17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
A z reszty tego czyni boga, swój posąg. Pada przed nim, oddaje mu pokłon i modli się do niego, mówiąc: Ratuj mnie, bo ty jesteś moim bogiem.
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
Nie wiedzą ani nie rozumieją, bo [Bóg] zaślepił ich oczy, aby nie widzieli, i ich serca, aby nie rozumieli.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
I nie rozważają tego w swoim sercu, nie mają wiedzy ani rozumu, by powiedzieć: Część tego spaliłem w ogniu, a na węglu z tego wypiekłem chleb, upiekłem mięso i najadłem się. Czyż z reszty tego mam uczynić coś obrzydliwego? Czyż mam padać przed klocem drzewa?
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
Taki się karmi popiołem, jego zwiedzione serce wprowadziło go w błąd, tak że nie może wybawić swojej duszy ani powiedzieć: Czyż nie jest fałszem to, co znajduje się w mojej prawicy?
21 Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
Pamiętaj o tym, Jakubie i Izraelu, gdyż jesteś moim sługą. Stworzyłem cię, jesteś moim sługą. O Izraelu, nie zapomnę o tobie.
22 Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
Zmazałem twoje nieprawości jak obłok, a twoje grzechy jak mgłę. Nawróć się do mnie, bo cię odkupiłem.
23 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
Śpiewajcie, niebiosa, bo PAN to uczynił. Wykrzykujcie, głębiny ziemi. Rozbrzmiewajcie śpiewaniem góry, lesie wraz ze wszystkimi drzewami; PAN bowiem odkupił Jakuba, a w Izraelu okrył się chwałą.
24 Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
Tak mówi PAN, twój Odkupiciel, który cię stworzył już od łona matki: Ja, PAN, wszystko czynię: sam rozciągam niebiosa, rozpościeram ziemię swoją mocą;
25 Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
Wniwecz obracam znaki kłamców i z wróżbitów czynię szaleńców; mędrców zmuszam do odwrotu, a ich wiedzę czynię głupstwem.
26 Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
Potwierdzam słowa swego sługi i spełniam radę swoich posłańców. Ja mówię do Jerozolimy: Będziesz zamieszkana, do miast Judy: Będziecie odbudowane, bo podniosę jej ruiny;
27 Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
To ja mówię głębinie: Wysychaj, ja wysuszę twoje potoki;
28 Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”
I o Cyrusie mówię: On jest moim pasterzem, bo wypełni całą moją wolę; i mówię do Jerozolimy: Będziesz odbudowana, a do świątyni: Będziesz założona.