< Yesaya 44 >
1 Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
“Kodwa khathesi lalela, wena Jakhobe, nceku yami, Israyeli, engikukhethileyo.
2 Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
Nanku akutshoyo uThixo, yena owakwenzayo, owakubumba esiswini, njalo yena ozakusiza, uthi: Ungesabi, wena Jakhobe, nceku yami, Jeshuruni engikukhethileyo.
3 Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
Ngoba ngizathela amanzi elizweni elomileyo, lezifula emhlabathini owomileyo. Ngizathela uMoya wami phezu kwenzalo yakho lezibusiso zami phezu kwezizukulwane zakho.
4 Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
Zizahluma njengotshani emadlelweni, lanjengeminyezane ezifuleni ezigelezayo.
5 Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
Omunye uzakuthi, ‘Mina ngingokaThixo’; lomunye azibize ngebizo likaJakhobe; omunye laye uzaloba esandleni sakhe ukuthi, ‘OkaThixo,’ azinike ibizo lika-Israyeli.”
6 “Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
“Nanku akutshoyo uThixo, iNkosi loMhlengi ka-Israyeli, uThixo uSomandla: Mina ngingowokuqala njalo ngingowokucina; ngaphandle kwami kakho uNkulunkulu.
7 Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
Pho ngubani onjengami? Kakumemezele lokho. Katsho, achaze phambi kwami okwenzakalayo kusukela ekubekeni kwami abantu bami bendulo; akutsho lokuzakwenzakala; yebo, kakuqambe okuzayo.
8 Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
Lingaqhaqhazeli, lingesabi. Lokhu angikutshongo ngabika ngakho kudala na? Lina lingofakazi bami. Kulomunye uNkulunkulu ngaphandle kwami na? Hatshi, kalikho elinye iDwala; kalikho engilaziyo.”
9 Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
Bonke abenza izithombe kabasilutho, lezinto abaziqakathekisayo ziyize. Labo abangabakhulumela bayiziphofu, kabazi lutho, kulihlazo kubo.
10 Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
Ngubani obaza unkulunkulu abumbe isithombe, okungeke kumsize ngalutho?
11 Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
Yena labanjengaye bazayangiswa; izingcitshi kazisilutho, ngabantu nje. Kaziqoqane zonke zime ndawonye; bazakuba lokwesaba kanye lehlazo.
12 Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
Umkhandi uthatha insimbi ayifake emalahleni; enze isithombe ngezando, asikhande ngengalo yakhe elamandla. Uyalamba aphelelwe ngamandla. Anganathi manzi, amandla aphele.
13 Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
Umbazi welula intambo yokulinganisa asidwebe ngosungulo, asibaze ngetshizela, asidwebe ngensimbi ecijileyo, abaze umfanekiso womuntu, umuntu olobuhle bonke, ukuba sihlale endlini yokukhonzela.
14 Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
Ugamula isihlahla somsedari, loba athathe umsayiphresi kumbe umʼOkhi. Uyasikhulisa phakathi kwezihlahla zegusu, kumbe ahlanyele iphayini, izulu lisikhulise.
15 Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
Lapho-ke siba zinkuni zomuntu zokubasa; okunye kwaso uyathatha othe, ubasa umlilo abhekhe izinkwa. Kodwa, njalo, wenza unkulunkulu amkhonze; abaze isithombe asikhothamele.
16 Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
Ingxenye yezinkuni ubasa ngayo umlilo, apheke ngawo ukudla kwakhe. Ose inyama yakhe adle asuthe. Njalo uyotha umlilo athi, “Ha! Ngiyafudumala; ngiyawubona umlilo.”
17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
Ngeziseleyo wenza unkulunkulu, isithombe sakhe; uyasikhothamela, asikhonze. Uyakhuleka kuso athi, “Ngisindisa, ungunkulunkulu wami.”
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
Kabazi lutho, kabaqedisisi lutho; amehlo abo abhadiwe ukuze bangaboni lezingqondo zabo zivalekile ukuze bangaqedisisi.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
Kakho oke ame acabange, kakho olokwazi loba ukuzwisisa ukuba athi, “Ingxenye yazo ngabasa ngayo umlilo; ngaze ngabhekha izinkwa emalahleni awo, ngosa inyama ngayidla. Ngokuseleyo ngizakwenza into enengisayo na? Ngizasikhothamela na isigodo nje?”
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
Udla umlotha, inhliziyo ekhohlisekileyo iyamlahla, angeke azihlenge, kumbe athi, “Into le esesandleni sami sokudla kayisimanga na?”
21 Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
“Khumbula lezizinto, wena Jakhobe, ngoba uyinceku yami, wena Israyeli. Ngakubumba, uyinceku yami; wena Israyeli, angiyikukukhohlwa.
22 Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
Ngesule iziphambeko zakho njengeyezi, ngesula izono zakho njengenkungu yekuseni. Buyela kimi, ngoba ngikuhlengile.”
23 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
Hlabelelani ngentokozo, lina mazulu, ngoba uThixo usekwenzile lokhu; hlaba umkhosi, wena mhlaba ngaphansi. Tshayani ingoma lina zintaba, lina mahlathi lazozonke izihlahla zenu, ngoba uThixo usemhlengile uJakhobe, ubonakalisa udumo lwakhe ko-Israyeli.
24 Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
“Nanku akutshoyo uThixo, uMhlengi wakho, owakubumbayo esiswini: Mina nginguThixo, owenza izinto zonke, owenza amazulu eyedwa, owendlala umhlaba eyedwa,
25 Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
ofubisa izibonakaliso zabaphrofethi bamanga, enze izanuse zibe yizithutha, ochitha ulwazi lwezihlakaniphi alwenze lube yibuthutha,
26 Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
ofeza amazwi ezinceku zakhe aphelelise amacebo ezithunywa zakhe. Athi kulo iJerusalema, ‘Kuzahlalwa kulo,’ ngamadolobho akoJuda athi, ‘Azakwakhiwa.’ Ngamanxiwa awo uthi, ‘Ngizawavusa,’
27 Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
athi enzikini yamanzi, ‘Cima, ngizakomisa izifula zakho,’
28 Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”
athi ngoKhurosi, ‘Ungumelusi wami, uzafeza konke engikufunayo; uzakuthi ngeJerusalema, “Kalakhiwe futhi,” ngethempeli athi, “Izisekelo zalo kazakhiwe.”’”