< Yesaya 44 >
1 Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
Og hør nu, Jakob, min Tjener! og Israel, som jeg udvalgte!
2 Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
Saa siger Herren, som gjorde dig og dannede dig fra Modersliv, han, som hjælper dig: Frygt ikke, min Tjener Jakob! og du, Jeskurun, som jeg udvalgte!
3 Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
Thi jeg vil udgyde Vand paa det tørstige og Strømme paa det tørre; jeg vil udgyde min Aand over din Sæd og min Velsignelse over dine Børn,
4 Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
at de skulle opvokse midt i Græs, ligesom Pile ved Vandbække.
5 Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
Den ene skal sige: Jeg er Herrens, og den anden skal kalde Jakob ved Navn; og en tredje skal skrive med sin Haand: Jeg hører Herren til, og han skal nævne Israel som Hædersnavn.
6 “Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
Saa siger Herren, Israels Konge, og hans Genløser, den Herre Zebaoth: Jeg er den første, og jeg er den sidste, og der er ingen Gud uden jeg.
7 Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
Og hvo, er som jeg, at han kan kalde noget frem, at han kan kundgøre det og ordentlig beskikke det for mig, som jeg har gjort, lige siden jeg lod et evigt Folk fremstaa? og kunne de forkynde dem de tilkommende Ting, og det, som skal komme?
8 Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
Frygter ikke, og forfærdes ikke! har jeg ikke forlængst ladet dig høre det og kundgjort det? og I ere mine Vidner; mon der er en Gud uden jeg? der er ingen Klippe, jeg kender deri ikke.
9 Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
De, som danne udskaarne Billeder, de ere alle intet, og de Billeder, de elske, gavne intet; og de, som ere deres Vidner, se intet og fornemme intet, derfor skulle de beskæmmes.
10 Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
Hvo danner vel en Gud og støber et Billede, som gavner til intet?
11 Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
Se, alle dets Tilhængere skulle beskæmmes; thi Mestrene, de ere kun Mennesker; de skulle alle samle sig, blive staaende, frygte og blive beskæmmede til Hobe.
12 Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
Smeden bruger Mejselen til Jernet og arbejder ved Kul og danner det med Hamrene; han arbejder paa det med sin Arms Kraft; men lider han Hunger, saa er delingen Kraft i ham mere, og drikker han ikke Vand, vansmægter han.
13 Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
Tømmermanden udstrækker en Maalesnor over Træet, mærker det af med Rødkridt, gør det jævnt med Høvlene og afridser det med Cirkelen; og han gør det efter en Mands Skikkelse, efter et Menneskes Anseelse, til at bo i et Hus.
14 Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
Han gaar hen at afhugge sig Cedre og tager Cypres og Eg, og han bruger sin Styrke iblandt Træerne i Skoven; han planter Valbirk, og Regnen bringer den til at vokse.
15 Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
Saa tjener det Mennesket til Brændsel, og han tager deraf og varmer sig og tænder Ild og bager Brød; men han gør ogsaa en Gud deraf og tilbeder den, han gør et udskaaret Billede deraf og falder paa Knæ for det.
16 Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
Halvdelen deraf brænder han paa Ilden; ved Halvdelen deraf æder han Kød og steger en Steg og mættes; ja, han varmer sig og siger: Ah! jeg har varmet mig, jeg har set Ild
17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
Men det øvrige deraf gør han til en Gud, til sit udskaarne Billede; han falder paa Knæ for det og nedbøjer sig og beder til det og siger: Frels mig! thi du er min Gud.
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
De fornemme ikke og forstaa ikke; thi han har tilstrøget deres Øjne, at de ikke se, og deres Hjerter, at de ikke forstaa.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
Og ingen tager sig det til Hjerte, og der er hverken Kundskab eller Forstand til at sige: Jeg har opbrændt Halvdelen deraf paa Ilden og ligeledes bagt Brød paa Gløderne deraf, jeg har stegt Kød og ædt; skal jeg da gøre det øvrige deraf til en Vederstyggelighed? skal jeg falde paa Knæ for en Træklods?
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
Han sætter sin Hu til Aske, hans Hjerte er bedraget, og det har ført ham vild; og han redder ikke sin Sjæl og siger ikke: Er det ikke Bedrageri, som jeg holder i min højre Haand?
21 Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
Kom disse Ting i Hu, Jakob og Israel! thi du er min Tjener; jeg har dannet dig, du er min Tjener, Israel! du skal ikke glemmes af mig.
22 Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
Jeg har udslettet dine Overtrædelser som en Taage og dine Synder som en Sky; vend om til mig; thi jeg har igenløst dig.
23 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
Synger med Fryd, I Himle! thi Herren har gjort det; raaber med Glæde, I Jordens Dybder! I Bjerge, raaber med Fryd, Skov og hvert Træ derudi! thi Herren har genløst Jakob og beviser sig herligt i Israel.
24 Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
Saa siger Herren; som har genløst dig og dannet dig fra Moders Liv af: Jeg er Herren, som gør alting, den, som ene udspænder Himmelen og udbreder Jorden; — hvo er vel med mig? —
25 Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
den, som gør Løgnerens Tegn til intet og gør Spaamændene til Daarer; den, som tvinger de vise tilbage og gør deres Vidskab til Daarskab;
26 Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
den, som stadfæster sin Tjeners Ord og fuldkommer sine Sendebuds Raad, den, som siger til Jerusalem: Den skal beboes, og til Judas Stæder: De skulle bygges, og jeg vil oprejse dens øde Stæder;
27 Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
den, som siger til Dybet: Bliv tør, og dine Floder vil jeg udtørre;
28 Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”
den, som siger til Kyrus: Han er min Hyrde, og han skal fuldkomme al min Villie, og han skal sige til Jerusalem: Du skal bygges; og til Templet: Du skal grundfæstes.