< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Dar acum, astfel spune DOMNUL care te-a creat, Iacobe, şi cel care te-a format, Israele: Nu te teme, fiindcă te-am răscumpărat, te-am chemat pe nume, eşti al meu.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Când vei trece prin ape, eu voi fi cu tine, şi prin râuri, ele nu te vor inunda; când vei umbla prin foc, nu vei fi ars; nici flacăra nu se va aprinde pe tine.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Fiindcă eu sunt DOMNUL Dumnezeul tău, Cel Sfânt al lui Israel, Salvatorul tău; am dat Egiptul ca răscumpărare a ta, Etiopia şi Seba pentru tine.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Căci ai fost preţios înaintea ochilor mei, ai fost demn de cinste şi te-am iubit, de aceea voi da oameni pentru tine şi popoare pentru viaţa ta.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Nu te teme, căci eu sunt cu tine: Voi aduce sămânţa ta din est şi te voi aduna din vest;
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
Voi spune nordului: Renunţă; şi sudului: Nu reţine; adu pe fiii mei de departe şi pe fiicele mele de la marginile pământului;
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Pe fiecare ce este chemat cu numele meu, fiindcă l-am creat pentru gloria mea, l-am format; da, eu l-am făcut.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Aduceţi poporul orb care are ochi şi pe surzii care au urechi.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Să se strângă toate naţiunile şi să se adune toate popoarele, cine dintre ei poate vesti aceasta şi să ne arate lucrurile din urmă? Să îşi aducă martorii lor, ca să fie declaraţi drepţi, sau să audă şi să spună: Este Adevăr.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Voi sunteţi martorii mei, spune DOMNUL, şi servitorul meu pe care l-am ales, ca să mă cunoaşteţi şi să mă credeţi şi să înţelegeţi că eu sunt el: Înaintea mea nu a fost format niciun Dumnezeu, nici nu va fi după mine.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
Eu, chiar eu, sunt DOMNUL; şi în afară de mine nu este salvator.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
Am vestit şi am salvat şi am arătat, când nu era dumnezeu străin printre voi, de aceea voi sunteţi martorii mei, spune DOMNUL, că eu sunt Dumnezeu.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Da, înainte ca ziua să fie, eu sunt el; şi nu este nimeni care să scape din mâna mea, voi face [lucrare] şi cine i se va împotrivi?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Astfel spune DOMNUL, răscumpărătorul tău, Cel Sfânt al lui Israel: De dragul vostru am trimis în Babilon şi am doborât pe toţi nobilii lor şi pe caldeeni, al căror strigăt este în corăbii.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
Eu sunt DOMNUL, Cel Sfânt al vostru, creatorul lui Israel, Împăratul vostru.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Astfel spune DOMNUL, care face o cale prin mare şi o cărare în apele puternice;
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Care aduce carul şi calul, armata şi puterea; se vor culca împreună şi nu se vor [mai] ridica, au dispărut de tot, sunt stinşi precum câlţii.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Nu vă amintiţi lucrurile dinainte, nici nu luaţi aminte la lucrurile din vechime.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Iată, voi face un lucru nou; acum se va ivi; să nu cunoaşteţi voi aceasta? Voi face o cale în pustiu [şi] râuri în locul secetos.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
Fiara câmpului mă va onora, dragonii şi bufniţele, pentru că eu dau ape în pustiu [şi] râuri în deşert, pentru a da de băut poporului meu, alesul meu.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
Pe acest popor l-am format pentru mine; vor arăta lauda mea.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
Dar tu nu m-ai chemat, Iacobe, ci te-ai obosit de mine, Israele.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Nu mi-ai adus viţeii ofrandei tale arse, nici nu m-ai onorat cu sacrificiile tale. Nu te-am făcut să serveşti cu o ofrandă, nici nu te-am obosit cu tămâie.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Nu mi-ai cumpărat cu bani trestie dulce de zahăr, nici nu m-ai umplut cu grăsimea sacrificiilor tale, ci m-ai făcut să servesc cu păcatele tale, m-ai obosit cu nelegiuirile tale.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
Eu, chiar eu, sunt cel care am şters fărădelegile tale de dragul meu şi nu îmi voi aminti păcatele tale.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Adu-mi aminte, să pledăm împreună; vesteşte, ca să poţi fi declarat drept.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Tatăl tău dintâi a păcătuit şi învăţătorii tăi au încălcat legea împotriva mea.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
De aceea am spurcat pe prinţii sanctuarului şi l-am dat pe Iacob blestemului şi pe Israel ocărilor.

< Yesaya 43 >