< Yesaya 43 >
1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Israel, beginilah kata TUHAN, "Akulah yang menjadikan dan membentuk engkau, jangan takut, engkau pasti Kuselamatkan! Aku telah memanggil engkau dengan namamu, engkau adalah milik-Ku.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Bila engkau mengarungi air, Aku akan menyertai engkau, engkau tak akan tenggelam dalam kesukaran-kesukaranmu. Bila melalui api, engkau tak akan hangus, percobaan-percobaan berat tak akan mencelakakan engkau.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Sebab Akulah TUHAN, Allahmu, Allah kudus Israel, Penyelamatmu. Mesir Kuberikan sebagai tebusanmu, Sudan dan Syeba sebagai gantimu.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Engkau berharga di mata-Ku, Aku menghargai dan mengasihi engkau; maka Kuberikan manusia sebagai gantimu, bangsa-bangsa sebagai ganti nyawamu.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Jangan takut, sebab Aku melindungi engkau. Dari barat dan dari timur Kusuruh anak cucumu datang berkumpul.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
Kuperintahkan kepada utara dan selatan, supaya mereka segera dilepaskan. Biar anak-anakmu lelaki kembali dari jauh, dan anak-anakmu perempuan pulang dari ujung-ujung bumi.
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Sebab mereka semua telah dipanggil dengan nama-Ku, mereka Kuciptakan untuk mengagungkan Aku."
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Allah berkata, "Suruhlah tampil ke depan bangsa-Ku yang buta, sekalipun mempunyai mata; yang tuli, sekalipun mempunyai telinga.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Suruhlah semua bangsa berkumpul dan semua suku berhimpun. Siapakah di antara dewa-dewa mereka telah memberitahukan apa yang terjadi sekarang? Siapa di antaranya dapat meramalkan masa depan? Biarlah saksi-saksi mereka tampil, dan membuktikan bahwa mereka benar, supaya semua yang mendengar mereka berkata, bahwa memang demikian!
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Hai umat-Ku, kamulah saksi-saksi-Ku, kamu Kupilih menjadi hamba-hamba-Ku, supaya mengenal Aku dan percaya kepada-Ku, dan mengerti bahwa Akulah Allah. Aku Allah Yang Mahaesa, tak ada lainnya sebelum dan sesudah Aku.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
Aku sendirilah TUHAN, selain Aku tak ada yang menyelamatkan.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
Aku telah memberitahukannya kepadamu, Akulah yang menyelamatkan kamu, dan bukan ilah asing yang ada di antaramu; kamulah yang menjadi saksi-saksi-Ku. Dan Aku, Aku ini Allah,
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
untuk selamanya Aku tetap Allah. Tak ada yang dapat luput dari kuasa-Ku, atau menghalangi rencana-Ku."
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
TUHAN Penyelamatmu, Yang Kudus Israel, berkata, "Demi kamu, Aku mengirim tentara ke Babel, dan Kudobrak palang-palang pintu penjara; sorak-sorai orang Kasdim Kuubah menjadi ratapan.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
Akulah TUHAN, Allahmu yang kudus, Rajamu, yang menciptakan engkau, hai Israel!"
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
TUHAN telah membuat sebuah jalan melalui laut, melalui air yang bergelora.
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Ia menyuruh tentara dan perwira-perwiranya berperang, dan mereka maju dengan kereta berkuda. Tetapi mereka jatuh, tak dapat bangkit lagi, mereka mati seperti sumbu yang padam.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
TUHAN berkata, "Tak ada gunanya mengingat masa lalu, percuma mengenang yang sudah-sudah.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Perhatikanlah, Aku membuat sesuatu yang baru; sekarang sudah mulai, tidakkah kaulihat? Aku akan membuat jalan di padang gurun, dan sungai-sungai di padang belantara.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
Binatang liar akan mengagungkan Aku; serigala dan burung unta akan memuji Aku sebab Aku mengalirkan air di padang gurun, dan sungai-sungai di padang belantara untuk memberi minum kepada umat pilihan-Ku.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
Merekalah bangsa yang Kubentuk bagi diri-Ku, agar dapat mewartakan pujian bagi-Ku."
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
TUHAN berkata, "Tetapi engkau Israel, tidak menyembah Aku, dan tidak lagi berbakti kepada-Ku.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Engkau tidak membawa domba untuk kurban bakaranmu, tidak menghormati Aku dengan persembahanmu. Padahal Aku tidak membebankan engkau dengan kurban, atau menyusahkan engkau dengan menuntut kemenyan.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Engkau tidak membeli dupa harum untuk-Ku, tidak memuaskan Aku dengan lemak kurban sembelihanmu. Sebaliknya engkau membebani Aku dengan dosa-dosamu, menyusahkan Aku dengan kesalahan-kesalahanmu.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
Namun Aku Allah yang menghapus dosamu, Aku mengampuni engkau karena begitulah sifat-Ku; Aku tidak mengingat-ingat dosamu.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Ingatkanlah Aku, mari kita ke pengadilan, adukan perkaramu supaya nyata bahwa engkau benar.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Nenek moyangmu yang pertama telah berdosa, para pemimpinmu telah memberontak terhadap Aku,
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
imam-imammu telah mencemarkan Rumah-Ku. Maka Israel Kuserahkan untuk dihina, keturunan Yakub Kubiarkan ditumpas."