< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Et maintenant, voici ce que dit le Seigneur, qui t’a créé, ô Jacob, et qui ta formé, ô Israël: Ne crains point, parce que je t’ai racheté, et appelé par ton nom; tu es mien, toi.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Lorsque tu passeras au travers des eaux, je serai avec toi, et les fleuves ne te submergeront pas; lorsque tu marcheras dans le feu, tu ne seras pas brûlé; et la flamme n’aura pas d’ardeur pour toi;
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Parce que je suis le Seigneur ton Dieu, le saint d’Israël, ton Sauveur; j’ai donné pour toi, afin de t’être propice, l’Egypte, l’Ethiopie et Saba.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Depuis que tu es devenu honorable à mes yeux et glorieux, moi, je t’ai aimé; je donnerai des hommes pour toi, et des peuples pour ton âme.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Ne crains point, parce que moi je suis avec toi; de l’Orient je ramènerai ta race; et de l’Occident je te rassemblerai.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
Je dirai à l’aquilon: Donne; et au midi: Ne retiens pas; amène mes fils de loin, et mes filles des extrémités de la terre.
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Car quiconque invoque mon nom, je l’ai créé pour ma gloire, je l’ai formé, et je l’ai fait.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Fais sortir un peuple aveugle et qui a des yeux; sourd, et il a des oreilles.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Toutes les nations se sont réunies ensemble, et des tribus se sont liées; qui parmi vous annoncera cela, et nous fera entendre les choses qui furent les premières? qu’ils produisent leurs témoins, qu’ils se justifient, et qu’ils entendent, et qu’ils disent: C’est vrai.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Vous êtes mes témoins, dit le Seigneur, vous et mon serviteur que j’ai choisi; afin que vous sachiez, que vous me croyiez, et que vous compreniez que c’est moi-même qui suis. Avant moi il n’y a pas eu de Dieu formé, et après moi il n’y en aura pas.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
C’est moi qui suis, c’est moi qui suis le Seigneur; et il n’y a pas, hors moi, de sauveur.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
C’est moi qui ai annoncé, et qui ai sauvé; j’ai fait entendre, et il n’y a pas eu parmi vous d’étranger; vous êtes mes témoins, dit le Seigneur, et moi, je suis Dieu.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Et dès le commencement je suis, et il n’y a personne qui arrache de ma main; j’agirai, et qui m’en détournera?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Voici ce que dit le Seigneur, votre rédempteur, le saint d’Israël: À cause de vous j’ai envoyé à Babylone, et j’ai arraché toutes ses barres, et les Chaldéens qui se glorifiaient dans leurs vaisseaux.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
Je suis le Seigneur, votre saint, le créateur d’Israël, votre roi.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Voici ce que dit le Seigneur, qui a fait dans la mer une voie, et au milieu des eaux impétueuses un sentier.
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Qui a fait sortir le quadrige et le cheval, l’armée et le fort; ils se sont endormis ensemble, ils ne se relèveront pas; ils ont été brisés comme le lin, et ils se sont éteints.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Ne vous souvenez plus des choses passées, et les anciennes, ne les regardez pas.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Voici que moi je fais des choses nouvelles; c’est maintenant qu’elles paraîtront; certainement vous les connaîtrez; je ferai dans le désert une voie, et dans un chemin impraticable des fleuves.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
La bête des champs me glorifiera, ainsi que les dragons et les autruches, parce que j’ai mis dans le désert des eaux, des fleuves dans un chemin impraticable, afin de donner à boire à mon peuple, à mon élu.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
J’ai formé ce peuple pour moi; il publiera ma louange.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
Cependant tu ne m’as pas invoqué, Jacob, et tu n’as pas travaillé pour moi, Israël.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Tu ne m’as pas offert ton bélier d’holocauste, et par tes victimes tu ne m’as pas glorifié; je ne t’ai pas forcé à me faire des oblations, et je ne t’ai pas donné la peine de m’offrir de l’encens.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Tu ne m’as pas acheté avec ton argent de canne odorante, et de la graisse de tes victimes tu ne m’as pas rassasié; mais tu m’as rendu ton esclave par tes péchés; tu m’as donné du mal par tes iniquités.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
C’est moi, c’est moi-même qui efface tes iniquités à cause de moi; et de tes péchés je ne me souviendrai pas.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Remets-moi en mémoire, et plaidons ensemble; raconte, si tu as quelque chose pour te justifier.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Ton père le premier a péché, et tes interprètes ont prévariqué contre moi.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
C’est pourquoi j’ai déclaré souillés les princes saints; j’ai livré Jacob à la tuerie, et Israël à l’outrage.

< Yesaya 43 >