< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
And now thus he says Yahweh [who] created you O Jacob and [who] formed you O Israel may not you be afraid for I have redeemed you I have called [you] by name your [belong] to me you.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
If you will pass in the waters [will be] with you I and in the rivers not they will overflow you if you will walk in fire not you will be burned and flame not it will burn you.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
For I [am] Yahweh God your [the] holy [one] of Israel deliverer your I have given ransom your Egypt Cush and Seba in place of you.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Because you are precious in view my you are honored and I I love you and I may give humankind in place of you and peoples in place of life your.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
May not you be afraid for [am] with you I from [the] east I will bring offspring your and from [the] west I will gather you.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
I will say to the north deliver up and to [the] south may not you withhold bring sons my from a distance and daughters my from [the] end of the earth.
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Every [one who] is called by name my and [whom] for glory my I created him [whom] I formed him also I made him.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Bring out a people blind and [are] eyes there and deaf [people] and ears [belong] to them.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
All the nations they have assembled together so they may gather peoples who? among them will he declare this and former [things] will they proclaim to? us let them appoint witnesses their so they may be justified and they may hear and they may say truth.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
You [are] witnesses my [the] utterance of Yahweh and servant my whom I have chosen so that you may know and you may believe me and you may perceive that I [am] he before me not it was formed a god and after me not it will be.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
I I [am] Yahweh and there not except me [is] a deliverer.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
I I have declared and I have saved and I have proclaimed and there not among you [was] a strange [god] and you [are] witnesses my [the] utterance of Yahweh and I [am] God.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Also from a day I [am] he and there not from hand my [is] a deliverer I act and who? will he revoke it.
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Thus he says Yahweh redeemer your [the] holy [one] of Israel for sake your I have sent Babylon towards and I will bring down [as] fugitives all of them and [the] Chaldeans in ships shout of joy their.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
I [am] Yahweh holy [one] your [the] creator of Israel king your.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Thus he says Yahweh who made in the sea a way and in waters mighty a path.
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Who sent out chariotry and horse[s] an army and a strong [one] together they lay down not they rose they were extinguished like wick they were quenched.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
May not you remember former [things] and ancient [things] may not you consider.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Here I [am] about to do a new [thing] now it is springing up ¿ not do you know it also I will make in the wilderness a way in a desolate place rivers.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
It honors me [the] animal[s] of the field jackals and daughters of an ostrich for I have put in the wilderness water rivers in a desolate place to give drink to people my chosen one my.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
A people which I formed for myself praise my they will recount.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
And not me you have called on O Jacob for you have grown weary with me O Israel.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Not you have brought to me [the] sheep of burnt offerings your and sacrifices your not you have honored me not I have burdened you with offering[s] and not I have made weary you with frankincense.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Not you have bought for me for money calamus and [the] fat of sacrifices your not you have satisfied me nevertheless you have burdened me with sins your you have made weary me with iniquities your.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
I I [am] he [who is] wiping out transgressions your for own sake my and sins your not I will remember.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Cause to remember me let us enter into judgment together recount O you so that you may be justified.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Ancestor your first he sinned and spokesmen your they transgressed against me.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
So I may profane [the] officials of holiness and I will give to total destruction Jacob and Israel to reviling words.

< Yesaya 43 >