< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
But now thus hath said the Lord that created thee, O Jacob, and he that formed thee, O Israel, Fear not; for I have redeemed thee, I have called thee by thy name; mine art thou.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Whenever thou passest through the waters, I am with thee; and through the rivers, —they shall not overflow thee: whenever thou walkest through the fire, thou shalt not be scorched; neither shall the flame burn on thee.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
For I am the Lord thy God, the Holy One of Israel, thy Saviour; I have given Egypt for thy ransom, Cush and Seba in place of thee.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Since thou art precious in my eyes, art honorable, and I indeed do love thee: therefore will I give men in place of thee, and nations instead of thy soul.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Fear not, for I am with thee; from the east will I bring thy seed, and from the west will I gather thee.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
I will say to the north, Give up; and to the south, Withhold not: bring my sons from afar, and my daughters from the ends of the earth;
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Every one that is called by my name, and whom I have created for my glory; whom I have formed; yea, whom I have made.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Bring forward the blind people that have eyes, and the deaf that have ears.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Let all the nations be gathered together, and let the people be assembled: who among them can announce this? and cause us to hear former things? let them bring forth their witnesses, that they may be justified: or let them hear, and say, It is truth.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Ye are my witnesses, saith the Lord, and my servant whom I have chosen: in order that ye may know and believe me, and understand, that I am he; before me there was no god formed, and after me there will be none.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
I, I am the Lord; and beside me there is no saviour.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
I myself have announced it, and I have saved, and I have let it be heard, and there was no strange [god] among you; and ye are my witnesses, saith the Lord, and I am God.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Yea, from the [first] day am I he; and there is none that can deliver out of my hand: if I will work, is there one that can hinder it?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Thus hath said the Lord, the Holy One of Israel, For your sake did I send to Babylon, and in swift vessels brought I them all down, and the Chaldeans, in the ships of their joyful song.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
I am the Lord, the Holy One, the Creator of Israel, your King.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Thus hath said the Lord, who maketh a way in the sea, and a path in the mighty waters;
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Who bringeth forth chariot and horse, army and power: together shall they lie down, they shall not rise up again; they are extinct, like a wick are they quenched.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Remember not the former things, and ancient events regard no more.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Behold, I will do a new thing; now shall it spring forth; will ye not acknowledge it? I will even make in the wilderness a way, and in the desert rivers.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
The beasts of the field shall honor me, the monsters and the ostriches; because I give waters in the wilderness, rivers in the desert, to give drink to my people, my elect;
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
This people which I have formed for myself; my praise shall they relate.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
But on me hast thou not called, O Jacob; for thou art become weary of me, O Israel.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Thou hast not brought unto me the lamb of thy burnt-offerings; and with thy sacrifices hast thou not honored me: I have not troubled thee with meat-offerings, nor wearied thee with frankincense.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Thou hast not bought for me sweet cane, and with the fat of thy sacrifices hast thou not satisfied me; but thou hast troubled me with thy sins, thou hast wearied me with thy iniquities.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
I, it is I that blot out thy transgressions for my own sake, and thy sins I will not remember.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Put me in remembrance; let us plead together: relate thou, in order that thou mayest be justified.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Thy first father did sin, and they that plead for thee transgressed against me.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
Therefore do I profane the holy princes, and I give up Jacob to the curse, and Israel to reproaches.

< Yesaya 43 >