< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
And now thus saith the Lord that created thee, O Jacob, and formed thee, O Israel: Fear not, for I have redeemed thee, and called thee by thy name: thou art mine.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
When thou shalt pass through the waters, I will be with thee, and the rivers shall not cover thee: when thou shalt walk in the fire, thou shalt not be burnt, and the flames shall not burn in thee:
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
For I am the Lord thy God, the Holy One of Israel, thy Saviour: I have given Egypt for thy atonement, Ethiopia and Saba for thee.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Since thou becamest honourable in my eyes, thou art glorious: I have loved thee, and I will give men for thee, and people for thy life.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Fear not, for I am with thee: I will. bring thy seed from the east, and gather thee from the west.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
I will say to the north: Give up: and to the south: Keep not back: bring my sons from afar, and my daughters from the ends of the earth.
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
And every one that calleth upon my name, I have created him for my glory, I have formed him, and made him.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Bring forth the people that are blind, and have eyes: that are deaf, and have ears.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
All the nations are assembled together, and the tribes are gathered: who among you can declare this, and shall make us hear the former things? let them bring forth their witnesses, let them be justified, and hear, and say: It is truth.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
You are my witnesses, saith the Lord, and my servant whom I have chosen: that you may know, and believe me, and understand that I myself am. Before me there was no God formed, and after me there shall be none.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
I am, I am the Lord: and there is no saviour besides me.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
I have declared, and have saved. I have made it heard, and there was no strange one among you. You are my witnesses, saith the Lord, and I am God.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
And from the beginning I am the same, and there is none that can deliver out of my hand: I will work, and who shall turn it away?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Thus saith the Lord your redeemer, the Holy One of Israel: For your sake I sent to Babylon, and have brought down all their bars, and the Chaldeans glorying in their ships.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
I am the Lord your Holy One, the Creator of Israel, your King.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Thus saith the Lord, who made a way in the sea, and a path in the mighty waters.
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Who brought forth the chariot and the horse, the army and the strong: they lay down to sleep together, and they shall not rise again: they are broken as flax, and are extinct.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Remember not former things, and look not on things of old.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Behold I do new things, and now they shall spring forth, verily you shall know them: I will make a way in the wilderness, and rivers in the desert.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
The beast of the field shall glorify me, the dragons and the ostriches: because I have given waters in the wilderness, rivers in the desert, to give drink to my people, to my chosen.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
This people have I formed for myself, they shall shew forth my praise.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
But thou hast not called upon me, O Jacob, neither hast thou laboured about me, O Israel.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Thou hast not offered me the ram of thy holocaust, nor hast thou glorified me with thy victims: I have not caused thee to serve with oblations, nor wearied thee with incense.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Thou hast bought me no sweet cane with money, neither hast thou filled me with the fat of thy victims. But thou hast made me to serve with thy sins, thou hast wearied me with thy iniquities.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
I am, I am he that blot out thy iniquities for my own sake, and I will not remember thy sins.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Put me in remembrance, and let us plead together: tell if thou hast any thing to justify thyself.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Thy brat father sinned, and thy teachers have transgressed against me.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
And I have profaned the holy princes, I have given Jacob to slaughter, and Israel to reproach.

< Yesaya 43 >