< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
А сега, така казва Господ Творецът ти, Якове, И създателят ти, Израилю: Не бой се, защото Аз те изкупих, Призовах те по име, Мой си ти
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Когато минаваш през водите, с тебе ще бъда, И през реките, те не ще те потопят; Когато ходиш през огъня, ти няма да се изгориш, И пламъкът не ще те опали.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Защото Аз съм Иеова твоят Бог, Светият Израилев, твоят Спасител; За твой откуп дадох Египет, За тебе Етиопия и Сева.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Понеже ти бе скъпоценен пред очите Ми, И почетен, и аз те възлюбих, Затова ще дам човеци а тебе, И племена за живота ти.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Не бой се, защото Аз съм с тебе; От изток ще доведа потомството ти, И от запад ще те събера;
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
Ще река на севера: Възвърни, И на юга: Не задържай; Доведи синовете Ми от далеч, И дъщерите Ми от земния край,
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Всички, които се наричат с Моето име, Които сътворих за славата Си; Аз създадох всеки от тях, да! Аз го направих.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Изведи слепите люде, които имат очи, И глухите, които имат уши.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Нека се съберат заедно всичките народи, И нека се стекат племената; Кой от тях може да възвести това и да ни обясни предишните събития? Нека доведат свидетелите си, за да се оправдаят Та да чуят човеците и да рекат: Това е вярно
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Вие сте Мои свидетели, казва Господ, И служителят Ми, когото избрах, За да Ме познаете и да повярвате в Мене, И да разберете, че съм Аз, - Че преди Мене не е имало Бог. И подир Мене няма да има.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
Аз, Аз съм Господ; И освен Мене няма спасител
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
Аз възвестих, и спасих, и показах, Когато не е имало между вас чужд Бог; Затова вие сте Ми свидетели, казва Господ, Че Аз съм Бог.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Да, преди да е имало време, Аз съм; И няма кой да избави от ръката Ми; Аз действувам, и кой ще Ми попречи?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Така казва Господ, вашият Изкупител, Светият Израилев; Заради вас пратих във Вавилон, И ще доведа всички като бежанци, Дори халдеите, в корабите, с които се хвалеха.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
Аз съм Господ, Светият ваш, Творецът Израилев, ваш Цар.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Така казва Господ, Който прави път в морето, И пътека в буйните води,
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
Който извежда колесници и коне, войска и сила: Те всички ще легнат, няма да станат; Унищожиха се, угаснаха като фитил.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Не си спомняйте предишните неща, Нито мислете за древните събития.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Ето, Аз ще направя ново нещо; Сега ще се появи; не ще ли внимавате в него? Да ще направя път в пустинята, И реки в безводната земя.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
Полските зверове ще Ме прославят, - Чакалите и камилоптиците, - Защото давам вода в пустинята, Реки в безводната земя, За да напоя людете Си, избраните Си,
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
Людете, които създадох за Себе Си, За да оповестяват хвалата Ми.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
Но ти Якове, не Ме призова; Но ти Израилю, се отегчи от Мене,
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Не си Ми принасял агънцата на всеизгарянията си, Нито си Ме почитал с жертвите си. Аз не те заробих с приноси, И не ти дотегнах с ливан.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Не си купил за Мене благоуханна тръстика с пари, Нито си Ме наситил с тлъстината на жертвите си; Но си Ме заробил с греховете си Дотегнал си Ми с беззаконията си,
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
Аз, Аз съм, Който изтривам твоите престъпления заради Себе Си, И няма да си спомня за греховете ти.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Подсети Ме, за да се съдим заедно; Представи делото си, за да се оправдаеш.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Твоят праотец съгреши, И учителите ти престъпиха против Мене.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
Затова ще сваля от свещенството им великите служители на светилището. И ще обрека Якова на изтребление, И ще направя Израиля за поругание.

< Yesaya 43 >