< Yesaya 42 >

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Оце Слуга Мій, що Я підпира́ю Його, Мій Обра́нець, що Його полюбила душа Моя. Я злив Свого Духа на Ньо́го, і Він правосу́ддя наро́дам пода́сть.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Він не буде кричати, і кли́кати не буде, і на ву́лицях чути не дасть Свого го́лосу.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
Він очерети́ни надло́мленої не доло́мить, і ґнота тлі́ючого не пога́сить, буде суд видавати за правдою.
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
Не вто́миться Він, і не знемо́жеться, поки при́суду не покладе на землі, і будуть чекати Зако́на Його острови́.
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
Говорить отак Бог, Господь, що створив небеса́ і їх розтягну́в, що землю простя́г та все те, що із неї вихо́дить, що наро́дові на ній Він диха́ння дає, і духа всім тим, хто ходить по ній.
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
Я, Господь, покли́кав Тебе в справедли́вості, і буду міцно трима́ти за ру́ки Тебе, і Тебе берегти́му, і дам Я Тебе заповітом наро́дові, за Світло пога́нам,
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
щоб очі відкрити незрячим, щоб ви́вести в'я́зня з в'язни́ці, а з темни́ці — тих ме́шканців те́мряви!
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
Я Господь, — оце Йме́ння Моє, і іншому слави Своєї не дам, ні хва́ли Своєї божка́м.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Речі давні прийшли ось, нові́ ж Я пові́м, дам почу́ти вам про них, поки ви́ростуть.
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Заспівайте для Господа пісню нову́, від кра́ю землі Йому хва́лу! Нехай шумить море, і все, що є в ньо́му, острови́ та їхні ме́шканці!
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
Хай голосно кличуть пустиня й міста́ її, осе́лі, що в них проживав Кеда́р! Хай виспі́вують ме́шканці скелі, хай кричать із верши́ни гірсько́ї!
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Нехай Го́споду честь віддаду́ть, і на острова́х Його славу звіща́ють!
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
Господь ви́йде, як ли́цар, розбу́дить завзя́ття Своє, як воя́к, піді́йме Він окрик та буде кричати, — переможе Своїх ворогів!
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
Я відві́ку мовчав, мовчазни́й був та стри́мувався, а тепер Я крича́тиму, мов породі́лля! буду тя́жко зідхати й хапа́ти повітря!
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
Спусто́шу Я го́ри й підгі́рки, і всі їхні зілля́ посушу́, і річки́ оберну́ в острови́, і стави́ повису́шую!
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
І Я попрова́джу незрячих дорогою, якої не знають, стежка́ми незна́ними їх поведу́, оберну́ перед ними темно́ту на світло, а нері́вне — в рівни́ну. Оце речі, які Я зроблю́, і їх не поки́ну!
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
Відсту́плять наза́д, посоро́мляться со́ромом ті, хто надію склада́в на божка́, хто бовва́нам казав: Ви наші боги!
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
Почуйте, глухі, а незря́чі, прозрі́те, щоб бачити!
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Хто сліпий, як не раб Мій, а глухий, як посол Мій, що Я посилаю його́? Хто сліпий, як дові́рений, і сліпий, як раб Господа?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Ти бачив багато, але не зберіг, мав ву́ха відкри́ті, але́ не почув.
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
Господь захоті́в був того ради правди Своєї, збільши́в та просла́вив Зако́на.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
Але він наро́д попусто́шений та поплюндро́ваний: усі вони по пече́рах пов'я́зані та по в'язни́цях похо́вані; стали вони за грабі́ж, і немає визво́льника, за здобич, й немає того, хто б сказав: Поверни́!
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Хто з вас ві́зьме оце до вух, на майбутнє почує й послу́хає?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
Хто Якова дав на здобич, а Ізраїля грабіжника́м? Хіба ж не Госпо́дь, що ми проти Нього грі́шили були́ і не хотіли ходи́ти путя́ми Його, а Зако́на Його ми не слу́хали?
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
І Він ви́лив на нього жар гніву Свого́ та наси́лля війни, що палахкоті́ло навко́ло його, — та він не пізна́в, і в ньому горіло воно, — та не брав він до се́рця цього́!

< Yesaya 42 >