< Yesaya 42 >

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
“Me somfo a mahyɛ no den ni, nea mayi no na ɔsɔ mʼani; mede me Honhom begu no so na ɔde atɛntrenee bɛbrɛ aman no.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Ɔrenteɛ mu anaa ɔremma ne nne so. Ɔremma ne nne so wɔ mmɔnten so.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
Demmire a ayɛ mmerɛw no, ɔremmu mu. Kanea ntamabamma a ɛnnɛw yiye no, ɔrennum. Nokware mu na ɔbɛda trenee adi;
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
ɔrenhinhim na ɔrempa abaw kosi sɛ ɔde trenee bɛba asase so. Ne mmara so na amanaman no de wɔn ani bɛto.”
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
Sɛɛ na Onyankopɔn, Awurade no se, nea ɔbɔɔ ɔsoro na ɔtrɛw mu, nea ɔtwee asase mu ne nea efi mu nyinaa, nea ɔma wɔn a wɔte so home, na ɔma wɔn a wɔnantew so no nkwa:
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
“Me, Awurade, mafrɛ wo trenee mu; meso wo nsa. Mɛhwɛ wo so na mede wo ayɛ apam ama nkurɔfo no ne kanea ama amanamanmufo,
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
na woabue ani a afura, na woayi nneduafo afi afiase na woagye wɔn a wɔda afiase amoa mu, wɔn a wɔte sum kabii mu no.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
“Mene Awurade; me din ne no! Meremfa mʼanuonyam mma obi anaa mʼayeyi mma ahoni.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Hwɛ, nneɛma dedaw no asisi, na nneɛma foforo no mepae mu ka; ansa na ɛbɛba mu no, meka kyerɛ mo.”
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Monto dwom foforo mma Awurade! Nʼayeyi mfi asase ano, mo a mokɔ po so ne nea ɛwo mu nyinaa, mo asupɔw ne wɔn a wɔtete so nyinaa.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
Ma nweatam ne so nkurow mma wɔn nne so; ma atenae a Kedar te so no nsɛpɛw wɔn ho. Ma nnipa a wɔwɔ Sela nto nnwom nnye wɔn ani; ma wɔnteɛ mu mfi mmepɔw no atifi!
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Ma wɔnhyɛ Awurade anuonyam; na wɔmpae mu nka nʼayeyi no wɔ asupɔw no so.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
Awurade bepue aba sɛ ɔkatakyi, te sɛ ɔkofo no, ɔbɛhyɛ ne mmɔdemmɔ mu den; ɔde nteɛmu bɛyɛ ɔkofo nkanyan na obedi nʼatamfo so nkonim.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
“Mayɛ komm akyɛ, mayɛ dinn na mahyɛ me ho so. Nanso afei, te sɛ ɔbea a ɔrewo no, meteɛ mu, mehome a ensi so na mehome afrɛ so.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
Mɛsɛe mmepɔw ne nkoko no na mahyew so afifide nyinaa. Mɛdan nsubɔnten ama ayɛ asupɔw, na mama atare ayoyow.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
Medi anifuraefo anim afa akwan a wonnim so so, akwan a wonnim so papa so na mɛkyerɛ wɔn kwan. Mɛma sum no ayɛ hann wɔ wɔn anim, na mayɛ mmeae a ɛyɛ abonkyiabonkyi no trontrom. Eyinom ne nneɛma a mɛyɛ; merennyaw wɔn mu.
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
Na wɔn a wɔde wɔn ho to ahoni so, na wɔka kyerɛ nsɛsode se, ‘Moyɛ yɛn anyame’ no, wɔbɛpam wɔn wɔ animguase mu.”
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
“Tie, wo ɔsotifo; hwɛ, wo onifuraefo na hu!
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Hena ne onifuraefo sɛ me somfo, na ɔyɛ ɔsotifo sɛ ɔbɔfo a mesoma no? Hena na nʼani afura sɛ nea ɔde ne werɛ ahyɛ me mu, nʼani afura sɛ Awurade somfo?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Woahu nneɛma bebree, nanso amfa wo ho; Ɔkwan da wʼasom, nanso wonte hwee.”
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
Ɛsɔɔ Awurade ani, ne trenee nti sɛ ɔbɛma ne mmara ayɛ kɛse na anya anuonyam.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
Nanso saa nnipa a wɔawia wɔn na wɔafow wɔn yi, wɔn nyinaa aka amoa mu anaa wɔde wɔn asie wɔ afiase. Wɔayɛ wɔn asade na wonni obi a obegye wɔn; wɔayɛ wɔn akorɔnne na wonni obi a ɔbɛka se, “Momfa wɔn nsan nkɔ.”
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Mo mu hena na obetie eyi anaa nʼani beku ho yiye akyiri yi?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
Hena na ɔde Yakob maa sɛ ɔmmɛyɛ akorɔnne, na ɔde Israel maa afowfo? Ɛnyɛ Awurade a yɛayɛ bɔne atia no no? Efisɛ wɔannantew nʼakwan so; na wɔanni ne mmara so.
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
Enti ohwiee nʼabufuwhyew guu wɔn so, akodi mu basabasayɛ. Ɛde ogyaframa bunkam wɔn so, nanso wɔante ase. Ɛhyew wɔn, nanso amfa wɔn ho.

< Yesaya 42 >