< Yesaya 42 >

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Voici mon serviteur, je le soutiendrai; mon élu, en qui s’est complue mon âme; j’ai répandu mon esprit sur lui; il annoncera la justice aux nations.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Il ne criera point, il ne fera acception de personne; sa voix ne sera pas entendue au dehors.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
Il ne brisera pas un roseau froissé, il n’éteindra pas une mèche fumante: il jugera dans la vérité.
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
Une sera point triste, ni précipité, jusqu’à ce qu’il établisse sur la terre la justice; et les îles attendront sa loi.
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
Voici ce que dit le Seigneur Dieu, qui a créé les cieux et les a étendus; qui a affermi la terre et ce qui en germe; qui a donné le souffle au peuple qui est sur elle, et la respiration à ceux qui la foulent aux pieds.
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
Moi, le Seigneur, je t’ai appelé dans la justice, et je t’ai pris par la main et je t’ai conservé. Et je t’ai établi pour être l’alliance du peuple, la lumière des nations;
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
Afin d’ouvrir les yeux des aveugles, de retirer du cachot le captif enchaîné, du fond de leur prison ceux qui étaient assis dans les ténèbres.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
Je suis le Seigneur, c’est là mon nom; je ne donnerai pas ma gloire à un autre, et la louange qui m’appartient aux images taillées au ciseau.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Les premiers événements, voici qu’ils sont arrivés; j’en annonce aussi de nouveaux; avant qu’ils arrivent, je vous les ferai connaître.
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Chantez au Seigneur un cantique nouveau, et sa louange des extrémités de la terre, vous qui descendez sur la mer, et ce qu’elle renferme, îles, et vous, leurs habitants.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
Que le désert et ses cités se lèvent; dans des maisons habitera Cédar; louez, habitants de Pétra; du sommet des montagnes ils crieront.
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Ils donneront au Seigneur la gloire, et ils annonceront sa louange dans les îles.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
Le Seigneur comme un brave sortira; comme un homme qui marche au combat il excitera le zèle; il élèvera la voix, et jettera des cris; contre ses ennemis il se fortifiera.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
Je me suis toujours tu, j’ai gardé le silence; j’ai été patient; comme la femme en travail, je parlerai; je détruirai, j’engloutirai tout à la fois.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
Je rendrai désertes les montagnes et les collines, et je dessécherai leur verdure; je changerai les fleuves en îles, et les étangs, je les tarirai.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
Et je conduirai les aveugles dans une voie qu’ils ne connaissent pas; et dans les sentiers qu’ils ignorent, je les ferai marcher; je convertirai devant eux les ténèbres en lumière, et les chemins tortus en chemins droits; j’ai fait ces choses pour eux, et je ne les ai pas délaissés.
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
Ils sont retournés en arrière; qu’ils soient entièrement couverts de confusion, ceux qui se confient dans leur image taillée au ciseau, qui disent à une statue jetée en fonte: Vous êtes nos dieux.
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
Sourds, écoutez; aveugles, regardez pour voir.
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Qui est aveugle, sinon mon serviteur? et sourd, sinon celui à qui j’ai envoyé mes messagers? qui est aveugle, sinon celui qui a été vendu? et qui est aveugle, sinon le serviteur du Seigneur?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Toi qui vois beaucoup de choses, n’observeras-tu point? toi qui as les oreilles ouvertes, n’entendras-tu point?
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
Et le Seigneur a voulu le sanctifier, et magnifier la loi, et en relever la grandeur.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
Mais le peuple lui-même a été pillé et ravagé; tous sont devenus un lacs pour les jeunes hommes; et au fond des prisons ils ont été cachés; ils sont devenus la proie de l’ennemi, et il n’est personne qui les délivre; ils ont été livrés au pillage, et il n’est personne qui dise: Rends.
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Qui est celui parmi vous qui écoute cela, qui y soit attentif, et ait foi aux choses futures?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
Qui a livré Jacob en proie, et Israël à ceux qui le ravagent? n’est-ce pas le Seigneur lui-même, contre qui nous avons péché? Et ils n’ont pas voulu marcher dans ses voies, et ils n’ont pas écouté sa loi.
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
Et il a lancé sur eux l’indignation de sa fureur, et une forte guerre; il a allumé un feu autour de lui, et il ne l’a pas su; il l’a livré aux flammes, et il n’a pas compris.

< Yesaya 42 >