< Yesaya 42 >
1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Lo! my seruaunt, Y schal vptake hym, my chosun, my soule pleside to it silf in hym. I yaf my spirit on hym, he schal brynge forth doom to hethene men.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
He schal not crie, nether he schal take a persoone, nether his vois schal be herd withoutforth.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
He schal not breke a schakun rehed, and he schal not quenche smokynge flax; he schal brynge out doom in treuthe.
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
He schal not be sorewful, nether troblid, til he sette doom in erthe, and ilis schulen abide his lawe.
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
The Lord God seith these thingis, makynge heuenes of noyt, and stretchynge forth tho, makynge stidfast the erthe, and tho thingis that buriownen of it, yyuynge breeth to the puple, that is on it, and yyuynge spirit to hem that treden on it.
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
Y the Lord haue clepid thee in riytfulnesse, and Y took thin hond, and kepte thee, and Y yaf thee in to a boond of pees of the puple, and in to liyt of folkis.
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
That thou schuldist opene the iyen of blynde men; that thou schuldist lede out of closyng togidere a boundun man, fro the hous of prisoun men sittynge in derknessis.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
Y am the Lord, this is my name; Y schal not yyue my glorie to an othere, and my preisyng to grauun ymagis.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Lo! tho thingis that weren the firste, ben comun, and Y telle newe thingis; Y schal make herd to you, bifore that tho bigynnen to be maad.
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Synge ye a newe song to the Lord; his heriyng is fro the laste partis of erthe; ye that goon doun in to the see, and the fulnesse therof, ilis, and the dwelleris of tho.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
The desert be reisid, and the citees therof; he schal dwelle in the housis of Cedar; ye dwelleris of the stoon, herie ye; thei schulen crie fro the cop of hillis.
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Thei schulen sette glorie to the Lord, and they schulen telle his heriyng in ilis.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
The Lord as a strong man schal go out, as a man a werryour he schal reise feruent loue; he schal speke, and schal crie; he schal be coumfortid on hise enemyes.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
Y was stille, euere Y helde silence; Y was pacient, Y schal speke as a womman trauelynge of child; Y schal scatere, and Y schal swolowe togidere.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
Y schal make desert hiy mounteyns and litle hillis, and Y schal drie vp al the buriownyng of tho; and Y schal sette floodis in to ilis, and Y schal make poondis drie.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
And Y schal lede out blynde men in to the weie, which thei knowen not, and Y schal make hem to go in pathis, whiche thei knewen not; Y schal sette the derknessis of hem bifore hem in to liyt, and schrewid thingis in to riytful thingis; Y dide these wordis to hem, and Y forsook not hem.
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
Thei ben turned abac; be thei schent with schenschipe, that trusten in a grauun ymage; whiche seien to a yotun ymage, Ye ben oure goddis.
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
Ye deef men, here; and ye blynde men, biholde to se.
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Who is blynd, no but my seruaunt? and deef, no but he to whom Y sente my messangeris? Who is blynd, no but he that is seeld? and who is blynd, no but the seruaunt of the Lord?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Whether thou that seest many thingis, schalt not kepe? Whether thou that hast open eeris, schalt not here?
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
And the Lord wolde, that he schulde halewe it, and magnefie the lawe, and enhaunse it.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
But thilke puple was rauyschid, and wastid; alle thei ben the snare of yonge men, and ben hid in the housis of prisouns. Thei ben maad in to raueyn, and noon is that delyuereth; in to rauyschyng, and noon is that seith, Yelde thou.
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Who is among you, that herith this, perseyueth, and herkneth thingis to comynge?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
Who yaf Jacob in to rauyschyng, and Israel to distrieris? Whether not the Lord? He it is, ayens whom thei synneden; and thei nolden go in hise weies, and thei herden not his lawe.
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
And he schedde out on hem the indignacioun of his strong veniaunce, and strong batel; and thei brenten it in cumpas, and it knewe not; and he brente it, and it vndurstood not.