< Yesaya 41 >
1 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
I Øer! tier for mig; og Folkene forny deres Kraft! lad dem komme, lad dem da tale; lader os træde frem for Retten med hinanden!
2 “Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
Hvo har opvakt ham fra Østen, hvem Retfærdigheden møder, hvor han gaar? hvo hengav Folkefærd for hans Ansigt og Kongerne, at han herskede over dem, hvilke hans Sværd gør som Støv og hans Bue som Halm, der bortblæses?
3 Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
Han forfølger dem, drager frem med Fred ad den Sti, som hans Fødder ikke have betraadt tilforn.
4 Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
Hvo udrettede og gjorde det? Han, som kalder Slægterne fra Begyndelsen! jeg Herren er den første, og med de sidste er jeg ogsaa.
5 Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
Øerne se det og frygte, Jordens Ender forfærdes; de nærme sig og komme.
6 aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
De hjælpe den ene den anden, og den ene siger til den anden: Staa fast!
7 Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
Tømmermanden sætter Mod i Guldsmeden, den, som glatter med Hammeren, i ham, som smeder paa Ambolten; „Sammenføjningen er god”, siger denne, og han befæster det med Søm, at det ikke rokkes.
8 “Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
Men du, Israel! du, min Tjener Jakob, som jeg udvalgte, Abrahams, min Vens, Sæd!
9 Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
du, hvem jeg hentede fra Jordens Ender og kaldte fra dens yderste Grænser, og til hvem jeg sagde: Du er min Tjener, jeg udvalgte dig og forkastede dig ikke!
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
Frygt ikke; thi jeg er med dig; se ikke ængstelig om; thi jeg er din Gud; jeg har styrket dig, ja, hjulpet dig, ja, holdt dig oppe med min Retfærdigheds højre Haand.
11 “Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
Se, alle de, som harmes paa dig, skulle beskæmmes og blive til Skamme; de Mænd, som trætte med dig, skulle blive til intet og omkomme.
12 Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
De Mænd, som kives med dig, skal du søge efter og ikke finde; de Mænd, som stride imod dig, skulle blive til intet og omkomme.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
Thi jeg er Herren din Gud, som tager dig ved din højre Haand, som siger til dig: Frygt ikke; jeg hjælper dig.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
Frygt ikke, du Orm, Jakob! du lille Hob, Israel! jeg hjælper dig, siger Herren, og din Frelser er Israels Hellige.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
Se, jeg gør dig til en skarp ny Tærskevogn med mange Tænder; du skal tærske og sønderknuse Bjerge og gøre Høje som Avner.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
Du skal kaste dem, og Vejret skal løfte dem, og en Storm skal adsprede dem; men du skal fryde dig i Herren, du skal prise dig i Israels Hellige.
17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
De elendige og de fattige lede efter Vand, og der er intet, deres Tunge forsmægter af Tørst; jeg, Herren, vil bønhøre dem, jeg, Israels Gud, vil ikke forlade dem.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
Jeg vil lade Floder bryde frem paa de nøgne Høje og Kilder midt i Dalene; jeg vil gøre Ørken til vandrig Sø og det tørre Land til Vandløb.
19 Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
Jeg vil i Ørken sætte Cedre, Sitimtræer og Myrtetræer og Olietræer; paa den slette Mark vil jeg sætte baade Fyrretræer, Kintræer og Buksbom,
20 kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
paa det at de skulle se og vide og baade lægge paa Hjerte og forstaa, at Herrens Haand har gjort dette, og Israels Hellige har skabt dette.
21 “Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
Kommer hid med eders Sag, siger Herren; kommer frem med eders stærke Bevisninger, siger Jakobs Konge.
22 Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
Lad dem komme frem med dem og forkynde os det, som skal hændes; forkynder os, hvad der først skal ske, paa det vi maa lægge os det paa Hjerte og forstaa, hvad Enden derpaa skal blive; eller lader os høre de tilkommende Ting!
23 tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
Forkynder de Ting, som skulle komme herefter, at vi kunne vide dem; thi I ere jo Guder! ja, gører vel eller gører ilde, saa ville vi se os om og betragte det med hverandre.
24 Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
Se, I ere intet, og eders Gerning er aldeles intet; den, som vælger eder, er en Vederstyggelighed.
25 “Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
Jeg har opvakt ham fra Norden, og han skal komme, ham fra Solens Opgang, som skal paakalde mit Navn; og han skal komme over Fyrsterne, som vare de Dynd, og som en Pottemager, der træder Ler.
26 Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
Hvo har forkyndt noget fra Begyndelsen af, at vi kunne vide det? eller fra forrige Tid, at vi kunne sige: Han har Ret? men der er ingen, som forkynder noget, og ingen, som lader os høre noget, og ingen, som hører eders Tale.
27 Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
Jeg er den første, som siger til Zion: Se, se, her ere de! og som bærer Jerusalem et godt Budskab.
28 Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
Ser jeg mig om, er der ingen, og af disse er der heller ingen Raadgiver, at jeg kunde spørge dem ad, og de kunde give Svar tilbage.
29 Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.
Se dem alle! deres Gerninger ere Daarlighed og Tomhed; deres støbte Billeder ere Vejr og Vind.