< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
Утіша́йте, втіша́йте наро́да Мого́, говорить ваш Бог!
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
Промовляйте до серця Єрусалиму, і закли́чте до нього, що ви́повнилась його доля тяжка́, що вина йому ви́бачена, що він за свої всі гріхи вдвоє взяв з руки Господа!
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
Голос кли́че: На пустині вготу́йте дорогу Господню, в степу ви́рівняйте битий шлях Богу нашому!
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Хай піді́йметься всяка доли́на, і хай зни́зиться всяка гора́ та підгі́рок, і хай стане круте́ за рівни́ну, а па́сма гірські́ — за доли́ну!
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
І з'я́виться слава Господня, і разом побачить її кожне тіло, бо у́ста Господні оце прорекли́!
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Голос кли́че: „Звіща́й!“Я ж спитав: „Про що буду звіща́ти? Всяке тіло — трава, всяка ж слава — як цвіт польови́й:
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
трава засихає, а квітка зів'я́не, як по́дих Господній пові́є на неї! Справді, наро́д — то трава:
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
Трава засихає, а квітка зів'я́не, Слово ж нашого Бога пові́ки стоя́тиме!
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
На го́ру високу зберися собі, благові́снику Сіону, свого голоса сильно підви́щ, благові́снику Єрусалиму! Підви́щ, не лякайся, скажи містам Юди: Ось Бог ваш!
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
Ось при́йде Господь, Бог, як сильний, і буде раме́но Його панувати для Ньо́го! Ось із Ним нагоро́да Його, а перед обличчям Його — відпла́та Його.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
Він ота́ру Свою буде па́сти, як Па́стир, раме́ном Своїм позбирає ягня́та, і на лоні Своє́му носи́тиме їх, дійнякі́в же прова́дити буде!
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
Хто во́ди помі́ряв своєю долонею, а п'я́дею ви́міряв небо, і трети́ною міри обняв пил землі, і гори ті зва́жив ваго́ю, а взгі́р'я — шалька́ми?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
Хто Господнього Духа збагну́в, і де́ та люди́на, що ради свої подава́ла Йому́?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
З ким ра́дився Він, і той напоу́мив Його, та навчав путі пра́ва, і пізна́ння навчив був Його, і Його напоу́мив дороги розумної?
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
Таж наро́ди — як кра́пля з відра́, а важать — як порох на ша́льках! Таж Він острови́ підіймає, немов ту пили́нку!
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
I Ливана не ви́стачить на запалі́ння жерто́вне, не стане й звір'я́ його на цілопа́лення!
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
Насу́проти Нього всі люди — немов би ніщо́, порахо́вані в Нього марно́тою та порожне́чею.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
І до ко́го вподо́бите Бога, і подобу яку ви поста́вите по́руч із Ним?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
Ма́йстер божка́ відлива́є, золота́р же його криє золотом, та виливає йому срібляні́ ланцюжки́.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
Убогий на да́ра такого бере собі дерево, що не гниє́, розшукує впра́вного ма́йстра, щоб поставив божка́, який не захита́ється.
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
Хіба ви не знаєте, чи ви не чули, чи вам не спові́щено зда́вна було́, чи ви не зрозуміли підва́лин землі?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
Він Той, Хто сидить понад кру́гом землі, а мешка́нці її — немов та сарана́. Він небо простя́г, мов ткани́ну тонку́, і розтягнув Він його, мов наме́та на ме́шкання.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
Він Той, Хто князі́в оберта́є в ніщо́, робить су́ддів землі за марно́ту:
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
вони не були ще поса́джені, і не були ще посі́яні, і пень їхній в землі ще не закоріни́вся, та як тільки на них Він дмухну́в, вони повсиха́ли, і буря поне́сла їх, мов ту солому!
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
І до кого Мене́ прирівня́єте, і йому́ буду рівний? говорить Святий.
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
Підійміть у височину́ ваші очі й побачте, хто те все створи́в? Той, Хто зо́рі виво́дить за їхнім числом та кличе ім'я́м їх усіх! І ніхто не загу́биться через всесильність та всемогу́тність Його́.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
По́що говориш ти, Якове, і кажеш, Ізраїлю: „Закрита доро́га моя перед Господом, і від Бога мого відійшло́ моє право“.
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
Хіба ж ти не знаєш, або ти не чув: Бог відві́чний — Господь, що кі́нці землі Він створи́в? Він не зму́чується та не вто́млюється, і не збагне́нний розум Його.
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
Він зму́ченому дає силу, а безси́лому — міць.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
І пому́чаться хлопці й пото́мляться, і юнаки́ спотикну́тись — спіткну́ться,
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
а ті, хто наді́ю склада́є на Господа, силу відно́влять, кри́ла піді́ймуть, немов ті орли́, будуть бігати — і не пото́мляться, будуть ходити — і не пому́чаться!

< Yesaya 40 >