< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
“Avutun halkımı” diyor Tanrınız, “Avutun!
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
Yeruşalim halkına dokunaklı sözler söyleyin. Angaryanın bittiğini, Suçlarının cezasını ödediklerini, Günahlarının cezasını RAB'bin elinden İki katıyla aldıklarını ilan edin.”
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
Şöyle haykırıyor bir ses: “Çölde RAB'bin yolunu hazırlayın, Bozkırda Tanrımız için düz bir yol açın.
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Her vadi yükseltilecek, Her dağ, her tepe alçaltılacak. Böylelikle engebeler düzleştirilecek, Sarp yerler ovaya dönüştürülecek.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
O zaman RAB'bin yüceliği görünecek, Bütün insanlar hep birlikte onu görecek. Bunu söyleyen RAB'dir.”
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Ses, “Duyur” diyor. “Neyi duyurayım?” diye soruyorum. “İnsan soyu ota benzer, Bütün vefası kır çiçeği gibidir.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
RAB'bin soluğu esince üzerlerine, Ot kurur, çiçek solar. Gerçekten de halk ottan farksızdır.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
Ot kurur, çiçek solar, Ama Tanrımız'ın sözü sonsuza dek durur.”
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
Ey Siyon'a müjde getiren, Yüksek dağa çık! Ey Yeruşalim'e müjde getiren, Yükselt sesini, bağır, Sesini yükselt, korkma. Yahuda kentlerine, “İşte, Tanrınız!” de.
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
İşte Egemen RAB gücüyle geliyor, Kudretiyle egemenlik sürecek. Ücreti kendisiyle birlikte, Ödülü önündedir.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
Sürüsünü çoban gibi güdecek, Kollarına alacak kuzuları, Bağrında taşıyacak; Usul usul yol gösterecek emziklilere.
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
Kim denizleri avucuyla, Gökleri karışıyla ölçebildi? Yerin toprağını ölçeğe sığdıran, Dağları kantarla, Tepeleri teraziyle tartabilen var mı?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
RAB'bin düşüncesine kim akıl erdirebildi? O'na öğüt verip öğretebilen var mı?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
Akıl almak, adalet yolunu öğrenmek için RAB kime danıştı ki? O'na bilgi veren, anlayış yolunu bildiren var mı?
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
RAB için uluslar kovada bir damla su, Terazideki toz zerreciği gibidir. Adaları ince toz gibi tartar.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
Adakları yakmaya yetmez Lübnan ormanı, Yakmalık sunu için az gelir hayvanları.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
RAB'bin önünde bütün uluslar bir hiç gibidir, Hiçten bile aşağı, değersiz sayılır.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
Öyleyse Tanrı'yı kime benzeteceksiniz? Neyle karşılaştıracaksınız O'nu?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
Putu döküm işçisi yapar, Kuyumcu altınla kaplar, Gümüş zincirler döker.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
Böyle bir sunuya gücü yetmeyen yoksul kişi Çürümez bir ağaç parçası seçer. Yerinden kımıldamaz bir put yapsın diye Usta bir işçi arar.
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
Bilmiyor musunuz, duymadınız mı? Başlangıçtan beri size bildirilmedi mi? Dünyanın temelleri atılalı beri anlamadınız mı?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
Gökkubbenin üstünde oturan RAB'dir, Yeryüzünde yaşayanlarsa çekirge gibidir. Gökleri perde gibi geren, Oturmak için çadır gibi kuran O'dur.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
O'dur önderleri bir hiç eden, Dünyanın egemenlerini sıfıra indirgeyen.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
O önderler ki, yeni dikilmiş, yeni ekilmiş ağaç gibi, Gövdeleri yere yeni kök salmışken RAB'bin soluğu onları kurutuverir, Kasırga saman gibi savurur.
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
“Beni kime benzeteceksiniz ki, Eşitim olsun?” diyor Kutsal Olan.
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
Başınızı kaldırıp göklere bakın. Kim yarattı bütün bunları? Yıldızları sırayla görünür kılıyor, Her birini adıyla çağırıyor. Büyük kudreti, üstün gücü sayesinde hepsi yerli yerinde duruyor.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
Ey Yakup soyu, ey İsrail! Neden, “RAB başıma gelenleri görmüyor, Tanrı hakkımı gözetmiyor?” diye yakınıyorsun?
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
Bilmiyor musun, duymadın mı? Ebedi Tanrı, RAB, bütün dünyayı yaratan, Ne yorulur ne de zayıflar, O'nun bilgisi kavranamaz.
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
Yorulanı güçlendirir, Takati olmayanın kudretini artırır.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
Gençler bile yorulup zayıf düşer, Yiğitler tökezleyip düşerler.
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
RAB'be umut bağlayanlarsa taze güce kavuşur, Kanat açıp yükselirler kartallar gibi. Koşar ama zayıf düşmez, Yürür ama yorulmazlar.

< Yesaya 40 >