< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
“Conforto, consolo meu povo”, diz seu Deus.
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
“Fale confortavelmente com Jerusalém, e chame-a para que sua guerra seja cumprida, que sua iniquidade seja perdoada, que ela tenha recebido da mão de Javé o dobro por todos os seus pecados”.
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
A voz de quem chama, “Prepare o caminho de Yahweh no deserto! Fazer uma rodovia nivelada no deserto para nosso Deus.
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Todo vale deve ser exaltado, e todas as montanhas e colinas devem ser baixadas. O desnível deve ser nivelado, e as asperezas colocam uma planície.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
A glória de Yahweh deve ser revelada, e toda a carne deve vê-lo junto; pois a boca de Iavé o disse”.
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
A voz de quem diz: “Grite!” Um disse: “O que eu devo chorar?”. “Toda a carne é como a grama, e toda sua glória é como a flor do campo.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
A grama murcha, a flor se desvanece, porque o fôlego de Yahweh sopra sobre ele. Certamente, as pessoas são como a grama.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
A grama murcha, a flor se desvanece; mas a palavra de nosso Deus permanece para sempre”.
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
Você que conta boas notícias a Zion, suba em uma montanha alta. Vocês que dão boas notícias a Jerusalém, levantem sua voz com força! Levantem-no! Não tenha medo! Diga às cidades de Judá: “Eis o seu Deus!”
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
Eis que o Senhor Yahweh virá como um poderoso, e seu braço irá governar por ele. Eis que sua recompensa está com ele, e sua recompensa perante ele.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
Ele alimentará seu rebanho como um pastor. Ele reunirá os cordeiros em seu braço, e carregá-las em seu seio. Ele conduzirá gentilmente aqueles que têm seus filhotes.
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
Quem mediu as águas no oco de sua mão, e marcou o céu com seu vão, e calculou o pó da terra em uma cesta de medição, e pesou as montanhas em balanças, e as colinas em equilíbrio?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
Que dirigiu o Espírito de Yahweh, ou o ensinou como seu conselheiro?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
Com quem ele se aconselhou, e quem o instruiu, e o ensinou no caminho da justiça, e lhe ensinou conhecimentos, e lhe mostrou o caminho para a compreensão?
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
Eis que as nações são como uma gota em um balde, e são considerados como um grão de pó sobre um equilíbrio. Eis que ele levanta as ilhas como uma coisinha muito pequena.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
O Líbano não é suficiente para queimar, nem seus animais são suficientes para uma oferta queimada.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
Todas as nações são como nada antes dele. Eles são considerados por ele como menos que nada, e vaidade.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
A quem, então, você vai gostar de Deus? Ou que semelhança você vai comparar com ele?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
Um operário lançou uma imagem, e o ourives a reveste com ouro, e funde correntes de prata para ele.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
Aquele que é demasiado empobrecido para tal oferta escolhe uma árvore que não apodreça. Ele procura um artesão hábil para montar uma imagem esculpida para ele que não será movida.
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
Você ainda não sabia? Você ainda não ouviu falar? Você não foi avisado desde o início? Você não entendeu desde os fundamentos da terra?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
É ele quem se senta acima do círculo da terra, e seus habitantes são como gafanhotos; que estica os céus como uma cortina, e as espalha como uma tenda para morar dentro,
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
que traz os príncipes ao nada, que torna os juízes da terra sem sentido.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
Eles são pouco plantados. Elas são semeadas dificilmente. Seu estoque quase não se enraizou no solo. Ele apenas sopra neles, e eles murcham, e o redemoinho os leva como restolho.
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
“A quem, então, você vai gostar de mim? Quem é meu igual?” diz o Santo.
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
Levante os olhos para o alto, e ver quem os criou, que traz à tona seu exército pelo número. Ele os chama a todos pelo nome. pela grandeza de seu poder, e porque ele é forte no poder, não falta nenhuma.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
Por que você diz, Jacob, e falar, Israel, “Meu caminho está escondido de Javé”, e a justiça que me é devida é desprezada pelo meu Deus”...
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
Você já não sabia? Você ainda não ouviu falar? O Deus eterno, Yahweh, o Criador dos confins do mundo, não desmaia. Ele não está cansado. Seu entendimento é indecifrável.
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
Ele dá poder aos fracos. Ele aumenta a força daquele que não tem poder.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
Even os jovens desmaiam e ficam cansados, e os jovens caem por completo;
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
mas aqueles que esperam por Yahweh renovarão suas forças. Eles se erguem com asas como águias. Eles correrão, e não se cansarão. Eles caminharão, e não desmaiarão.

< Yesaya 40 >