< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
خدای اسرائیل می‌فرماید: «تسلی دهید! قوم مرا تسلی دهید!
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
اهالی اورشلیم را دلداری دهید و به آنان بگویید که روزهای سخت ایشان به سر آمده و گناهانشان بخشیده شده، زیرا من به اندازهٔ گناهانشان آنها را تنبیه کرده‌ام.»
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
صدایی می‌شنوم که می‌گوید: «راهی از وسط بیابان برای آمدن خداوند آماده کنید. راه او را در صحرا صاف کنید.
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
دره‌ها را پر کنید؛ کوهها و تپه‌ها را هموار سازید؛ راههای کج را راست و جاده‌های ناهموار را صاف کنید.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
آنگاه شکوه و جلال خداوند ظاهر خواهد شد و همهٔ مردم آن را خواهند دید. خداوند این را وعده فرموده است.»
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
بار دیگر آن صدا می‌گوید: «با صدای بلند بگو!» پرسیدم: «با صدای بلند چه بگویم؟» گفت: «با صدای بلند بگو که انسان مانند علف است. تمام زیبایی او همچون گل صحراست که پژمرده می‌شود.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
وقتی خدا می‌دمد علف خشک می‌شود و گل پژمرده. بله، انسان مانند علف از بین می‌رود.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
گیاه خشک می‌شود و گل پژمرده می‌گردد، اما کلام خدای ما برای همیشه باقی می‌ماند.»
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
ای قاصد خوش خبر، از قلهٔ کوه، اورشلیم را صدا کن. پیامت را با تمام قدرت اعلام کن و نترس. به شهرهای یهودا بگو: «خدای شما می‌آید!»
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
بله، خداوند یهوه می‌آید تا با قدرت حکومت کند. پاداشش همراه او است و هر کس را مطابق اعمالش پاداش خواهد داد.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
او مانند شبان، گلهٔ خود را خواهد چرانید؛ بره‌ها را در آغوش خواهد گرفت و میشها را با ملایمت هدایت خواهد کرد.
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
آیا کسی غیر از خدا می‌تواند اقیانوس را در دست نگه دارد و یا آسمان را با وجب اندازه گیرد؟ آیا کسی غیر از او می‌تواند خاک زمین را در ترازو بریزد و یا کوهها و تپه‌ها را با قَپّان وزن کند؟
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
کیست که بتواند به روح خداوند پند دهد؟ کیست که بتواند معلم یا مشاور او باشد؟
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
آیا او تا به حال به دیگران محتاج بوده است که به او حکمت و دانش بیاموزند و راه راست را به او یاد دهند؟
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
به هیچ وجه! تمام مردم جهان در برابر او مثل قطرهٔ آبی در سطل و مانند غباری در ترازو، ناچیز هستند. همهٔ جزایر دنیا برای او گردی بیش نیستند و او می‌تواند آنها را از جایشان تکان دهد.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
اگر تمام حیوانات لبنان را برای خدا قربانی کنیم باز کم است و اگر تمام جنگلهای لبنان را برای روشن کردن آتش قربانی به کار بریم باز کافی نیست.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
تمام قومها در نظر او هیچ هستند و ناچیز به شمار می‌آیند.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
چگونه می‌توان خدا را توصیف کرد؟ او را با چه چیز می‌توان مقایسه نمود؟
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
آیا می‌توان او را با یک بت مقایسه کرد؟ بُتی که بت ساز آن را ساخته و با طلا پوشانده و به گردنش زنجیر نقره‌ای انداخته است؟
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
فقیری که نمی‌تواند خدایانی از طلا و نقره درست کند، درختی می‌یابد که چوبش با دوام باشد و آن را به دست صنعتگری ماهر می‌دهد تا برایش خدایی بسازد، خدایی که حتی قادر به حرکت نیست!
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
آیا تا به حال ندانسته‌اید و نشنیده‌اید و کسی به شما نگفته که دنیا چگونه به وجود آمده است؟
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
خدا دنیا را آفریده است؛ همان خدایی که بر فراز کرهٔ زمین نشسته و مردم روی زمین در نظر او مانند مورچه هستند. او آسمانها را مثل پرده پهن می‌کند و از آنها خیمه‌ای برای سکونت خود می‌سازد.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
او رهبران بزرگ دنیا را ساقط می‌کند و از بین می‌برد.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
هنوز ریشه نزده خدا بر آنها می‌دمد، و آنها پژمرده شده، مثل کاه پراکنده می‌گردند.
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
خداوند قدوس می‌پرسد: «شما مرا با چه کسی مقایسه می‌کنید؟ چه کسی می‌تواند با من برابری کند؟»
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
به آسمانها نگاه کنید! کیست که همهٔ این ستارگان را آفریده است؟ کسی که آنها را آفریده است از آنها مثل یک لشکر سان می‌بیند، تعدادشان را می‌داند و آنها را به نام می‌خواند. قدرت او آنقدر عظیم است که نمی‌گذارد هیچ‌کدام از آنها گم شوند.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
پس، ای اسرائیل، چرا می‌گویی خداوند رنجهای مرا نمی‌بیند و با من به انصاف رفتار نمی‌کند؟
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
آیا تا به حال ندانسته و نشنیده‌ای که یهوه خدای سرمدی، خالق تمام دنیا هرگز درمانده و خسته نمی‌شود و هیچ‌کس نمی‌تواند به عمق افکار او پی ببرد؟
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
او به خستگان نیرو می‌بخشد و به ضعیفان قدرت عطا می‌کند.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
حتی جوانان هم درمانده و خسته می‌شوند و دلاوران از پای در می‌آیند،
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
اما آنانی که به خداوند امید بسته‌اند نیروی تازه می‌یابند و مانند عقاب پرواز می‌کنند؛ می‌دوند و خسته نمی‌شوند، راه می‌روند و ناتوان نمی‌گردند.

< Yesaya 40 >