< Yesaya 40 >
1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
Consolez, consolez mon peuple, dit le Seigneur;
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
Prêtres, parlez au cœur de Jérusalem; consolez-la, car son humiliation est accomplie; son péché lui est remis, parce qu'elle a reçu de la main du Seigneur un châtiment double de ses péchés.
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
On entend la voix de celui qui crie dans le désert: Préparez la voie du Seigneur, redressez les sentiers de notre Dieu.
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Toute vallée sera remplie, toute montagne sera abaissée; les chemins tortueux seront redressés, ceux qui étaient raboteux seront aplanis.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
Et la gloire du Seigneur se manifestera, et toute chair verra le salut de Dieu; car le Seigneur a parlé.
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Une voix m'a dit: Crie; et j'ai répondu: Que crierai-je? Toute chair est de l'herbe; toute gloire humaine est comme la fleur des champs.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
L'herbe s'est desséchée, et la fleur est tombée.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
Mais la parole de notre Dieu subsistera dans tous les siècles.
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
Ô toi qui annonce à Sion la bonne nouvelle, monte sur le sommet de la montagne; élève la voix de toutes tes forces, toi qui annonce à Jérusalem la bonne nouvelle; dis-leur: Glorifiez-vous, ne craignez point; dis aux villes de Juda: Voilà votre Dieu.
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
Voilà le Seigneur, le Seigneur vient avec la force, son bras a la puissance; voilà dans ses mains le salaire, et l'œuvre est devant ses yeux.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
Il fera paître son troupeau comme un pasteur; il rassemblera les agneaux, et il encouragera les brebis pleines.
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
Qui a mesuré les eaux à la main, le ciel à la palme, et toute la terre à la poignée? Qui a placé les montagnes dans une balance? Qui a pesé les forêts?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
Qui sait la pensée du Seigneur? Qui a tenu conseil avec lui pour l'instruire?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
Avec qui a-t-il tenu conseil, et qui l'a instruit? Qui lui a enseigné le jugement? Qui lui a montré la voie de la sagesse?
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
Est-ce que toutes les nations ne sont pas à ses yeux comme la goutte d'eau qui s'échappe du vase? comme l'oscillation d'une balance? Ne seront- elles pas à ses yeux comme un peu de salive?
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
Le Liban ne suffirait pas pour un bûcher; tous les quadrupèdes ne suffiraient pas pour un holocauste.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
Toutes les nations sont comme un néant; elles sont comptées comme un néant à ses yeux.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
A qui avez-vous comparé le Seigneur? A quel simulacre l'avez-vous assimilé?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
Est-ce qu'un artisan a jamais fait son image? Est-ce qu'un fondeur, en jetant de l'or dans un moule, l'a fait en or et a reproduit sa ressemblance?
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
L'ouvrier a choisi un bois incorruptible; puis il cherche avec soin de quelle manière il posera sa statue, pour qu'elle ne soit point ébranlée.
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
Ne savez-vous pas cela? Ne l'avez-vous pas ouï dire? Ne vous l'a-t-on pas appris dès le commencement? Ne connaissez-vous pas les fondements de la terre?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
C'est lui qui tient dans sa main le cercle de la terre, et, comme une nuée de sauterelles, tous ceux qui l'habitent. C'est lui qui a posé les cieux comme une voûte, et qui les a tendus comme la tente où l'on s'abrite.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
C'est lui par qui règnent les princes, qui sont comme un néant devant lui. C'est lui qui a créé la terre et la regarde comme un néant.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
Car ces princes ne planteront pas, ils ne sèmeront pas, et leur racine ne prendra pas en terre. Il a soufflé sur eux, et ils se sont desséchés; la tempête les emportera comme des broussailles.
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
Maintenant donc, à qui m'avez-vous comparé, pour que je m'en glorifie? dit le Saint.
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
Levez les yeux et voyez; qui vous a montré toutes ces choses? C'est celui qui a produit les innombrables ornements des cieux qui dans sa gloire les appelle tous par leur nom, et qui, dans la plénitude de sa puissance, ne vous a rien caché.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
Et toi, qu'as-tu dit, Jacob? Pourquoi as-tu ainsi parlé, Israël? Ma voix est ignorée de Dieu, et mon Dieu m'a retiré sa justice, et il s'est éloigné.
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
Et maintenant n'as-tu pas appris, n'as-tu pas entendu? Dieu, c'est l'Éternel; c'est Dieu qui a assigné des limites à la terre; il ne sentira jamais la faim ni la fatigue; et il n'y a pas à pénétrer sa sagesse.
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
C'est lui qui donne la force aux affamés, et non la tristesse à ceux qui sont dans la douleur.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
Car les adolescents auront faim, les jeunes gens seront fatigués, les hommes d'élite seront affaiblis.
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
Mais ceux qui attendent le Seigneur trouveront des forces nouvelles; il leur poussera des ailes comme aux aiglons; ils courront, et ne seront point fatigués; ils marcheront, et n'auront pas faim.