< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
Lohduttakaat, lohduttakaat minun kansaani, sanoo teidän Jumalanne.
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
Puhukaat suloisesti Jerusalemin kanssa, ja saarnatkaat hänelle, että hänen sotimisensa on täytetty; sillä hänen rikoksensa on annettu anteeksi, että hän on saanut kaksinkertaisesti Herran kädestä, kaikkein synteinsä tähden.
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
Huutavaisen ääni on korvessa: valmistakaat Herran tietä, tehkäät tasaiset polut erämaassa meidän Jumalallemme.
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Kaikki laaksot pitää korotettaman, ja kaikki vuoret ja kukkulat pitää alennettaman, ja mitä on tasoittamatta, pitää tasattaman ja koliat silitettämän.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
Sillä Herran kunnia ilmoitetaan: ja kaikki liha on ynnä näkevä Herran suun puhuvan.
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Ääni sanoo: saarnaa. Ja hän sanoi: Mitä minun pitää saarnaaman? Kaikki liha on ruoho, ja kaikki hänen hyvyytensä niinkuin kedon kukkanen.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
Ruoho kuivuu pois ja kukkanen lakastuu, sillä Herra puhalsi siihen. Kansa tosin on ruoho.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
Ruoho kuivettuu ja kukkanen lakastuu; mutta meidän Jumalamme sana pysyy ijankaikkisesti.
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
Zion, sinä suloinen saarnaaja, astu korkialle vuorelle; Jerusalem, sinä suloinen saarnaaja, korota äänes väkevästi: korota ja älä pelkää; sano Juudan kaupungeille: katso, teidän Jumalanne.
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
Sillä katso, Herra, Herra tulee väkevyydessä, ja hänen käsivartensa on hallitseva: katso, hänen palkkansa on hänen myötänsä, ja hänen tekonsa on hänen edessänsä,
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
Niinkuin paimen on hän kaitseva laumaansa, kokoo karitsat syliinsä ja kantaa helmassansa: tiineet lampaat hän johdattaa.
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
Kuka on vedet pivollansa mitannut, ja käsittänyt vaaksallansa taivaat? ja maan tomun sulkenut kolmannekseen? ja vuoret puntarilla punninnut, ja kukkulat vaalla?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
Kuka on Herran henkeä opettanut? eli kuka on hänen neuvonantajansa ollut?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
Keneltä hän neuvoa kysyy, joka hänelle ymmärrystä antais, ja opettais hänelle oikeuden tien, ja antais hänelle tiedon, ja opetais hänelle ymmärryksen tien?
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
Katso, pakanat ovat niinkuin pisara, joka jää ämpäriin, ja niinkuin rahtu, joka jää vaakaan; katso, luodot hän kuljettaa niinkuin piskuisen tomun.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
Libanon olis sangen vähä tuleksi; ja hänen eläimensä ylen harvat polttouhriksi.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
Kaikki pakanat ovat niinkuin ei mitään hänen edessänsä, ja juuri tyhjän ja turhan edestä pidetään häneltä.
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
Keneenkä te tahdotte verrata Jumalaa? eli mitä kuvaa te tahdotte hänelle tehdä?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
Seppä valaa kuvan, ja hopiaseppä kultaa sen ja tekee siihen hopiakäädyt.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
Niin myös jolla vähä vara on tehdä ylennysuhria, hän valitsee puun, joka ei mätäne, ja etsii siihen taitavan tekiän valmistamaan kuvaa, joka on kestäväinen.
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
Ettekö te tiedä? ettekö te kuule? eikö tämä ole ennen teille ilmoitettu? ettekö te ole sitä ymmärtäneet maan alusta?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
Hän istuu maan piirin päällä, ja ne, jotka sen päällä asuvat, ovat niinkuin heinäsirkat; joka taivaan venyttää niinkuin ohukaisen nahan, ja levittää sen niinkuin teltan, asuttavaksi.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
Joka pääruhtinaat tyhjäksi tekee, ja hävittää tuomarit maan päältä,
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
Niinkuin ei he olisi istutetut, eikä kylvetyt, eli heidän kantonsa juurtuneet maahan; niin että he kuivettuvat, kuin tuuli heidän päällensä puhaltaa, ja tuulispää vie heidät matkaansa niinkuin akanat.
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
Keneenkä te siis minun verrata tahdotte, jonka kaltainen minä olisin? sanoo Pyhä.
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
Nostakaat silmänne korkeuteen ja katsokaat, kuka ne kappaleet luonut on, ja vie edes heidän joukkonsa luvulla? kutsuu ne kaikki nimeltänsä? Hänen varansa ja väkevä voimansa on niin suuri, ettei häneltä mitään puutu.
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
Miksis siis sinä Jakob sanot, ja sinä Israel puhut: minun tieni on Herralta salattu, ja minun oikeuteni käy minun Jumalani ohitse?
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
Etkös tiedä? etkös ole kuullut? Herra ijankaikkinen Jumala, joka maan ääret on luonut, ei väsy eikä näänny; hänen ymmärryksensä on tutkimatoin.
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
Hän antaa väsyneille voiman, ja väettömille kyllä väkeä.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
Nuorukaiset väsyvät ja nääntyvät, ja nuoret miehet peräti lankeevat;
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
Mutta jotka Herraa odottavat, ne saavat uuden voiman, niin että he menevät siivillä ylös kuin kotkat; että he juoksevat ja ei näänny, he vaeltavat ja ei väsy.

< Yesaya 40 >