< Yesaya 40 >

1 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
to be sorry: comfort to be sorry: comfort people my to say God your
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
to speak: speak upon heart Jerusalem and to call: call to to(wards) her for to fill army: war her for to accept iniquity: crime her for to take: recieve from hand LORD double in/on/with all sin her
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
voice to call: call out in/on/with wilderness to turn way: road LORD to smooth in/on/with plain highway to/for God our
4 Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
all valley to lift: raise and all mountain: mount and hill to abase and to be [the] steep to/for plain and [the] roughness to/for valley
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
and to reveal: reveal glory LORD and to see: see all flesh together for lip LORD to speak: speak
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
voice to say to call: call out and to say what? to call: call out all [the] flesh grass and all kindness his like/as flower [the] land: country
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
to wither grass to wither flower for spirit: breath LORD to blow in/on/with him surely grass [the] people
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
to wither grass to wither flower and word God our to arise: establish to/for forever: enduring
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
upon mountain: mount high to ascend: rise to/for you to bear tidings Zion to exalt in/on/with strength voice your to bear tidings Jerusalem to exalt not to fear to say to/for city Judah behold God your
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
behold Lord YHWH/God in/on/with strong to come (in): come and arm his to rule to/for him behold wages his with him and wages his to/for face: before his
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
like/as to pasture flock his to pasture in/on/with arm his to gather lamb and in/on/with bosom: embrace his to lift: bear to nurse to guide
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
who? to measure in/on/with handful his water and heaven in/on/with span to measure and to sustain in/on/with third dust [the] land: country/planet and to weigh in/on/with balance mountain: mount and hill in/on/with balance
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
who? to measure [obj] spirit LORD and man counsel his to know him
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
with who? to advise and to understand him and to learn: teach him in/on/with way justice and to learn: teach him knowledge and way: conduct understanding to know him
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
look! nation like/as drop from bucket and like/as cloud balance to devise: count look! coastland like/as thin to lift
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
and Lebanon nothing sufficiency to burn: burn and living thing his nothing sufficiency burnt offering
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
all [the] nation like/as nothing before him from end and formlessness to devise: count to/for him
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
and to(wards) who? to resemble [emph?] God and what? likeness to arrange to/for him
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
[the] idol to pour artificer and to refine in/on/with gold to beat him and chain silver: money to refine
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
[the] to impoverish contribution tree: wood not to rot to choose artificer wise to seek to/for him to/for to establish: establish idol not to shake
21 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
not to know not to hear: hear not to tell from head: first to/for you not to understand foundation [the] land: country/planet
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
[the] to dwell upon circle [the] land: country/planet and to dwell her like/as locust [the] to stretch like/as curtain heaven and to spread them like/as tent to/for to dwell
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
[the] to give: make to rule to/for nothing to judge land: country/planet like/as formlessness to make
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
also not to plant also not to sow also not to uproot in/on/with land: country/planet stock their and also to blow in/on/with them and to wither and tempest like/as stubble to lift: bear them
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
and to(wards) who? to resemble me and be like to say holy
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
to lift: look height eye your and to see: see who? to create these [the] to come out: send in/on/with number army their to/for all their in/on/with name to call: call to from abundance strength and strong strength man not to lack
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
to/for what? to say Jacob and to speak: speak Israel to hide way: conduct my from LORD and from God my justice my to pass
28 Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
not to know if: surely no not to hear: hear God forever: enduring LORD to create end [the] land: country/planet not to faint and not be weary/toil nothing search to/for understanding his
29 Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
to give: give to/for weary strength and to/for nothing strength strength to multiply
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
and to faint youth and be weary/toil and youth to stumble to stumble
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
and to await LORD to pass strength to ascend: rise wing like/as eagle to run: run and not be weary/toil to go: walk and not to faint

< Yesaya 40 >