< Yesaya 4 >

1 Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
Шапте фемей вор апука ын зиуа ачея ун сингур бэрбат ши вор зиче: „Вом мынка пыня ноастрэ ынсене ши не вом ымбрэка ын хайнеле ноастре ынсене; нумай фэ-не сэ-ць пуртэм нумеле ши я окара де песте ной!”
2 Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
Ын время ачея, одрасла Домнулуй ва фи плинэ де мэрецие ши славэ ши родул цэрий ва фи плин де стрэлучире ши фрумусеце пентру чей мынтуиць ай луй Исраел.
3 Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
Ши чел рэмас ын Сион, чел лэсат ын Иерусалим, се ва нуми „сфынт”, орьчине ва фи скрис принтре чей вий, ла Иерусалим.
4 Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
Дупэ че ва спэла Домнул мурдэрииле фийчелор Сионулуй ши ва курэци Иерусалимул де виновэция де сынӂе дин мижлокул луй, ку духул жудекэций ши ку духул нимичирий,
5 Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
Домнул ва ашеза, песте тоатэ ынтиндеря мунтелуй Сионулуй ши песте локуриле луй де адунаре, ун нор де фум зиуа ши ун фок де флэкэрь стрэлучитоаре ноаптя. Да, песте тоатэ слава ва фи ун адэпост,
6 Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.
о колибэ, ка умбрар ымпотрива кэлдурий зилей ши ка лок де адэпост ши де окротире ымпотрива фуртуний ши плоий.

< Yesaya 4 >