< Yesaya 4 >

1 Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
And seven women shall take hold of one man in that day, saying, Our own bread will we eat, and with our own garments will we be clothed; only let us be called by thy name; — take away our reproach!
2 Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
In that day there shall be a sprout of Jehovah for beauty and glory, and the fruit of the earth for excellency and for ornament for those that are escaped of Israel.
3 Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
And it shall come to pass that he who remaineth in Zion, and he that is left in Jerusalem, shall be called holy, — every one that is written among the living in Jerusalem;
4 Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
when the Lord shall have washed away the filth of the daughters of Zion, and shall have scoured out the blood of Jerusalem from its midst, by the spirit of judgment, and by the spirit of burning.
5 Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
And Jehovah will create over every dwelling-place of mount Zion, and over its convocations, a cloud by day and a smoke, and the brightness of a flame of fire by night: for over all the glory shall be a covering.
6 Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.
And there shall be a tabernacle for shade by day from the heat, and for a shelter and for a covert from storm and from rain.

< Yesaya 4 >