< Yesaya 4 >

1 Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
Syv Kvinder skal på hin Dag gribe fat i een Mand og sige: "Vi vil æde vort eget Brød og holde os selv med Klæder, blot vi må bære dit Navn. Tag Vanæren fra os!"
2 Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
På hin Dag Bliver HERRENs spire til Fryd og Ære og Landets Frugt til Stolthed og Smykke for de undslupne i Israel.
3 Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
Den, som er levnet i Zion og blevet tilovers i Jerusalem, skal kaldes hellig, enhver, der er indskrevet til Livet i Jerusalem,
4 Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
når Herren får aftvættet Zions Døtres Smuds og bortskyllet Jerusalems Blodskyld fra dets Midte med Doms og Udrensnings Ånd.
5 Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
Da skaber Herren over hvert et Sted på Zions Bjerg og over dets Festforsamlinger en Sky om Dagen og Røg med luende Ildskær om Natten; thi over alt, hvad herligt er, skal der være et Dække
6 Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.
og Ly til Skygge mod Hede og til Skærm og Skjul mod Skybrud og Regn.

< Yesaya 4 >