< Yesaya 39 >

1 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
Ngalesosikhathi uMerodaki-Baladani, indodana kaBaladani inkosi yeBhabhiloni, wathumela izincwadi lesipho kuHezekhiya, ngoba wayezwile ukuthi ubekade egula, useqinile.
2 Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
UHezekhiya wasethokoza ngazo, wabatshengisa indlu yokuligugu kwakhe, isiliva, legolide, lamakha, lamafutha amahle, lendlu yonke yezikhali zakhe, lakho konke okwatholakala kokuligugu kwakhe; kakubanga lalutho endlini yakhe lembusweni wakhe wonke uHezekhiya angabatshengisanga lona.
3 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Wasefika uIsaya umprofethi enkosini uHezekhiya, wathi kuyo: Atheni lamadoda? Futhi avele ngaphi esiza kuwe? UHezekhiya wasesithi: Avele elizweni elikhatshana esiza kimi, eBhabhiloni.
4 Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
Wasesithi: Aboneni endlini yakho? UHezekhiya wasesithi: Abone konke okusendlini yami; kakulalutho phakathi kokuligugu kwami engingawatshengisanga lona.
5 Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
UIsaya wasesithi kuHezekhiya: Zwana ilizwi leNkosi yamabandla.
6 Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
Khangela, insuku ziyeza lapho konke okusendlini yakho, lalokho oyihlo abakubuthelelayo kuze kube lamuhla, kuzathwalelwa eBhabhiloni; kakuyikusala lutho, kutsho iNkosi.
7 Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
Njalo bazathatha emadodaneni akho azaphuma kuwe, ozawazala; njalo abe ngabathenwa esigodlweni senkosi yeBhabhiloni.
8 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”
UHezekhiya wasesithi kuIsaya: Ilizwi leNkosi olikhulumileyo lilungile. Wathi futhi: Ngoba kuzakuba lokuthula leqiniso ensukwini zami.

< Yesaya 39 >