< Yesaya 39 >
1 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
At that time Merodach Baladan, the son of Baladan king of Babylon, sent letters and presents to Ezechias: for he had heard that he had been sick and was recovered.
2 Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
And Ezechias rejoiced at their coming, and he shewed them the storehouses of his aromatical spices, and of the silver, and of the gold, and of the sweet odours, and of the precious ointment, and all the storehouses of his furniture, and all things that were found in his treasures. There was nothing in his house, nor in all his dominion that Ezechias shewed them not.
3 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Then Isaias the prophet came to king Ezechias, and said to him: What said these men, and from whence came they to thee? And Ezechias said: From a far country they came to me, from Babylon.
4 Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
And he said: What saw they in thy house? And Ezechias said: All things that are in my house have they seen, there was not any thing which I have not shewn them in my treasures.
5 Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
And Isaias said to Ezechias: Rear the word of the Lord of hosts.
6 Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
Behold the days shall come, that all that is in thy house, and that thy fathers have laid up in store until this day, shall be carried away into Babylon: there shall not any thing be left, saith the Lord.
7 Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
And of thy children, that shall issue from thee, whom thou shalt beget, they shall take away, and they shall be eunuchs in the palace of the king of Babylon.
8 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”
And Ezechias said to Isaias: The word of the Lord, which he hath spoken, is good. And he said: Only let peace and truth be in my days.