< Yesaya 39 >

1 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
Te vaeng tue ah Hezekiah tlo tih koep a thoh te Babylon manghai Baladan capa Merodachbaladan loh a yaak tih ca neh khocang a pat.
2 Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
Hezekiah loh te te a kohoe tih a anhoi im khaw, a likmal khaw, cak neh sui khaw, botui neh situi then khaw, a im kah hnopai boeih te amih a tueng. A thakvoh khuikah a cungkuem te khaw a hmuh sak. A im neh a khohung pum kah aka om te Hezekiah loh amih a tueng pawh hno pakhat khaw om pawh.
3 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Te phoeiah tonghma Isaiah loh manghai Hezekiah te a paan tih, “Hekah hlang rhoek he balae a thui uh? Me lamkah lae nang taengla ha pawk uh,” a ti nah. Te dongah Hezekiah loh, “Khohla hmuen Babylon lamloh kai taengla ha pawk uh dae he,” a ti nah.
4 Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
Te phoeiah, “Na im ah balae a hmuh uh,” a ti nah hatah Hezekiah loh, “Ka im kah te boeih a hmuh uh. Ka thakvoh khuikah te amih ka tueng pawh hno pakhat khaw om pawh,” a ti nah.
5 Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
Te vaengah Isaiah loh Hezekiah te, “caempuei BOEIPA kah ol he hnatun lah.
6 Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
A khohnin ha pawk vaengah na im kah aka om boeih neh na pa rhoek loh tihnin duela a kael te khaw a phueih ni. Babylon loh hno pakhat khaw caknoi mahpawh, BOEIPA loh a thui.
7 Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
Namah lamkah na sak na ca rhoek lamloh aka thoeng rhoek te khaw a khuen uh vetih Babylon manghai bawkim ah imkhoem la poeh uh ni,” a ti nah.
8 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”
Hezekiah loh Isaiah taengah, “BOEIPA kah ol then ni na thui coeng te. Kamah tue vaengah ngaimong neh uepomnah om sak ham ni a thui dae,” a ti nah.

< Yesaya 39 >