< Yesaya 38 >
1 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
W one dni zachorował Ezechyjasz aż na śmierć. I przyszedł do niego Izajasz prorok, syn Amosowy, a rzekł do niego: Tak mówi Pan: Rozpraw dom swój; albowiem umrzesz, a nie zostaniesz żyw.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
Tedy obrócił Ezechyjasz twarz swoję do ściany, a modlił się Panu.
3 “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
I rzekł: Proszę, o Panie! wspomnij teraz, żem chodził przed tobą w prawdzie i w sercu uprzejmem, czyniąc to, co dobrego jest w oczach twoich. I płakał Ezechyjasz płaczem wielkim.
4 Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
I stało się słowo Pańskie do Izajasza, mówiąc:
5 “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
Idź, a powiedz Ezechyjaszowi: Tak mówi Pan, Bóg Dawida, ojca twego: Wysłuchałem modlitwę twoję, widziałem łzy twoje; oto Ja przyczynię do dni twoich piętnaście lat;
6 Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
I z ręki króla Assyryjskiego wyrwę ciebie i to miasto, a będę bronił miasta tego.
7 “‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
A to będziesz miał za znak od Pana, że Pan uczyni to, co mówił.
8 Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
Oto Ja wrócę nazad cień po stopniach po których szedł, na zegarze słonecznym Achazowym na dziesięć stopni po tychże stopniach, po których było zeszło.
9 Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
Pisanie Ezechyjasza, króla Judzkiego, gdy był zachorował i wyzdrowiał z niemocy swojej:
10 Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
Jam rzekł w ukróceniu dni moich: Wnijdę do bram grobu, pozbawion będę ostatka lat swoich; (Sheol )
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
Rzekłem, że nie ujrzę Pana, Pana w ziemi żyjących; nie oglądam więcej człowieka między obywatelami na świecie.
12 Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
Pobyt mój pomija, a przenosi się odemnie, jako namiot pasterski; oderznąłem żywot swój, jako tkacz; od krosien oderznie mię; dziś, pierwej niż noc nadejdzie, dokonasz mię.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
Rozmyślałem sobie z poranku, że jako lew potrze wszystkie kości moje, dziś, pierwej niż noc nadejdzie, dokonasz mię.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
Jako żóraw i jaskółka szczebiotałem, stękałem jako gołębica; oczy moje ku górze podniesione były, i rzekłem: Panie! gwałt cierpię, przedłuż mi żywota.
15 Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
Ale cóż mam więcej rzec? Onci mi odpowiedział, i sam uczynił, że żyć będę mimo wszystkie lata swe po gorzkości duszy mojej.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
Panie! kto po nich i w nich żyć będzie, wszystkim znajomy będzie żywot dychania mego, żeś mi zdrowie przywrócił, a zachowałeś mię przy żywocie.
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
Oto czasu pokoju przyszła na mię była gorzkość najgorzciejsza; ale się tobie podobało wyrwać duszę moję z przepaści skażenia, przeto, żeś zarzucił w tył swój wszystkie grzechy moje.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
Albowiem nie grób wysławia cię, ani śmierć chwali cię, ani ci, którzy w dół wstępują, oczekują prawdy twojej. (Sheol )
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
Żywy, żywy, ten cię wysławiać będzie, jako ja dzisiaj, a ojciec synom oznajmi prawdę twoję.
20 Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
Pan mię wybawił; przetoż pieśń moję śpiewać będziemy po wszystkie dni żywota naszego w domu Pańskim.
21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
I rzekł był Izajasz: Niech wezmą bryłę suchych fig, i przyłożą na wrzód, a będzie uzdrowiony.
22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”
I rzekł był Ezechyjasz: Cóż jest za znak, że wstąpię do domu Pańskiego?