< Yesaya 38 >
1 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
Ved den tid blev Esekias dødssyk; da kom profeten Esaias, Amos' sønn, inn til ham og sa til ham: Så sier Herren: Beskikk ditt hus! For du skal dø og ikke leve lenger.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
Da vendte Esekias sitt ansikt mot veggen og bad til Herren
3 “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
og sa: Akk, Herre! kom dog i hu at jeg har vandret for ditt åsyn i trofasthet og med helt hjerte og gjort hvad godt er i dine øine! Og Esekias gråt høit.
4 Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
Da kom Herrens ord til Esaias, og det lød så:
5 “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
Gå og si til Esekias: Så sier Herren, din far Davids Gud: Jeg har hørt din bønn, jeg har sett dine tårer; se, jeg legger femten år til din alder.
6 Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
Og jeg vil redde dig og denne by av assyrerkongens hånd, og jeg vil verne denne by.
7 “‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
Og dette skal du ha til tegn fra Herren på at Herren vil holde det han nu har lovt:
8 Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
Se, jeg lar solskivens skygge, som er gått ned med solen på Akas' solskive, gå ti streker tilbake. Og solen gikk tilbake ti av de streker den var gått ned.
9 Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
En sang, skrevet av Judas konge Esekias da han hadde vært syk, men hadde kommet sig av sin sykdom:
10 Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
Jeg sa: I mine rolige dager må jeg gå bort gjennem dødsrikets porter; jeg må bøte med resten av mine år. (Sheol )
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
Jeg sa: Jeg skal ikke se Herren, Herren i de levendes land jeg skal ikke skue mennesker mere blandt dem som bor i det stille.
12 Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
Min bolig blir rykket op og ført bort fra mig som en hyrdes telt; jeg har rullet mitt liv sammen lik en vever, fra trådendene skjærer han mig av; fra dag til natt gjør du det av med mig.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
Jeg fikk min sjel til å være stille inntil morgenen; som en løve knuser han alle mine ben; fra dag til natt gjør du det av med mig.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
Som en svale, som en trane, således klynket jeg, jeg kurret som en due; matte så mine øine mot det høie: Herre! Jeg er redd, gå i borgen for mig!
15 Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
Hvad skal jeg si? Han har både sagt mig det, og han har gjort det; stille vil jeg vandre alle mine år efter min sjels bitre smerte.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
Herre! Ved dem lever mennesket, og ved dem blir alt min ånds liv opholdt; så gjør mig frisk og la mig leve!
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
Se, til fred blev mig det bitre, ja det bitre, og kjærlig drog du min sjel op av tilintetgjørelsens grav; for du kastet alle mine synder bak din rygg.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
For ikke priser dødsriket dig, ikke lover døden dig; ikke venter de som farer ned i graven, på din trofasthet. (Sheol )
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
De levende, de levende, de priser dig, som jeg idag; en far lærer sine barn om din trofasthet.
20 Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
Herren er rede til å frelse mig, og på mine strengeleker vil vi spille alle vårt livs dager i Herrens hus.
21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
Esaias sa at de skulde hente en fikenkake og legge den som plaster på bylden, så han kunde bli frisk igjen.
22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”
Esekias sa: Hvad skal jeg ha til tegn på at jeg skal gå op til Herrens hus?