< Yesaya 38 >

1 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
In those days was Hezekiah sick and near death. Isaiah the prophet, the son of Amoz, came to him, and said to him, "Thus says the LORD, 'Set your house in order, for you will die, and not live.'"
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
Then Hezekiah turned his face to the wall and prayed to the LORD,
3 “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
and said, "Remember now, the LORD, I beg you, how I have walked before you in truth and with a perfect heart, and have done that which is good in your sight." Hezekiah wept bitterly.
4 Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
Then the word of the LORD came to Isaiah, saying,
5 “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
"Go, and tell Hezekiah, 'Thus says the LORD, the God of David your father, "I have heard your prayer. I have seen your tears. Look, I will add fifteen years to your life.
6 Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
I will deliver you and this city out of the hand of the king of Assyria, and I will defend this city.
7 “‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
This shall be the sign to you from the LORD, that the LORD will do this thing that he has spoken.
8 Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
Look, I will cause the shadow on the steps, which has gone down with the sun on the upper steps of Ahaz, to go backward ten steps. So the sun returned ten steps on the sundial on which it had gone down."'"
9 Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
The writing of Hezekiah king of Judah, when he had been sick, and had recovered of his sickness.
10 Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol h7585)
I said, "In the middle of my life I go into the gates of Sheol. I am deprived of the residue of my years." (Sheol h7585)
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
I said, "I won't see the LORD in the land of the living. I will not look on humankind any longer with the inhabitants of the world.
12 Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
My dwelling is removed, and is carried away from me like a shepherd's tent. I have rolled up, like a weaver, my life. He will cut me off from the loom. From day even to night you will make an end of me.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
I waited patiently until morning. He breaks all my bones like a lion. From day even to night you will make an end of me.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
I chip like a swallow or a thrush. I moan like a dove. My eyes weaken looking upward. LORD, I am oppressed. Be my security."
15 Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
What will I say? He has both spoken to me, and himself has done it. I will walk carefully all my years because of the anguish of my soul.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
The LORD is against them, but they live, and all of them who live have his spirit. Restore me to health and let me live.
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
Look, for peace I had great anguish, but you have in love for my soul delivered it from the pit of corruption; for you have cast all my sins behind your back.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol h7585)
For Sheol can't praise you. And death can't celebrate you. And those who go down into the pit can't hope for your truth. (Sheol h7585)
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
The living, the living, he shall praise you, as I do this day. The father shall make known your truth to the children.
20 Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
The LORD will save me. Therefore we will sing my songs with stringed instruments all the days of our life in the house of the LORD.
21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
Now Isaiah had said, "Let them take a cake of figs, and lay it for a poultice on the boil, and he shall recover."
22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”
Hezekiah also had said, "What is the sign that I will go up to the house of the LORD?"

< Yesaya 38 >