< Yesaya 38 >
1 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
In those days was Hezekiah sick unto death. And Isaiah the prophet the son of Amoz came to him, and said unto him: 'Thus saith the LORD: Set thy house in order; for thou shalt die, and not live.'
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
Then Hezekiah turned his face to the wall, and prayed unto the LORD,
3 “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
and said: 'Remember now, O LORD, I beseech Thee, how I have walked before Thee in truth and with a whole heart, and have done that which is good in Thy sight.' And Hezekiah wept sore.
4 Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
Then came the word of the LORD to Isaiah, saying:
5 “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
'Go, and say to Hezekiah: Thus saith the LORD, the God of David thy father: I have heard thy prayer, I have seen thy tears; behold, I will add unto thy days fifteen years.
6 Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
And I will deliver thee and this city out of the hand of the king of Assyria; and I will defend this city.
7 “‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
And this shall be the sign unto thee from the LORD, that the LORD will do this thing that He hath spoken:
8 Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
behold, I will cause the shadow of the dial, which is gone down on the sun-dial of Ahaz, to return backward ten degrees.' So the sun returned ten degrees, by which degrees it was gone down.
9 Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
The writing of Hezekiah king of Judah, when he had been sick, and was recovered of his sickness.
10 Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
I said: In the noontide of my days I shall go, even to the gates of the nether-world; I am deprived of the residue of my years. (Sheol )
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
I said: I shall not see the LORD, even the LORD in the land of the living; I shall behold man no more with the inhabitants of the world.
12 Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
My habitation is plucked up and carried away from me as a shepherd's tent; I have rolled up like a weaver my life; He will cut me off from the thrum; from day even to night wilt Thou make an end of me.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
The more I make myself like unto a lion until morning, the more it breaketh all my bones; from day even to night wilt Thou make an end of me.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
Like a swallow or a crane, so do I chatter, I do moan as a dove; mine eyes fail with looking upward. O LORD, I am oppressed, be Thou my surety.
15 Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
What shall I say? He hath both spoken unto me, and Himself hath done it; I shall go softly all my years for the bitterness of my soul.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
O Lord, by these things men live, and altogether therein is the life of my spirit; wherefore recover Thou me, and make me to live.
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
Behold, for my peace I had great bitterness; but Thou hast in love to my soul delivered it from the pit of corruption; for Thou hast cast all my sins behind Thy back.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
For the nether-world cannot praise Thee, death cannot celebrate Thee; they that go down into the pit cannot hope for Thy truth. (Sheol )
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
The living, the living, he shall praise Thee, as I do this day; the father to the children shall make known Thy truth.
20 Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
The LORD is ready to save me; therefore we will sing songs to the stringed instruments all the days of our life in the house of the LORD.
21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
And Isaiah said: 'Let them take a cake of figs, and lay it for a plaster upon the boil, and he shall recover.'
22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”
And Hezekiah said. 'What is the sign that I shall go up to the house of the LORD?'