< Yesaya 37 >

1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
Et il arriva que lorsque le roi Ezéchias les eut entendues, il déchira ses vêtements, et se couvrit d’un sac, et entra dans la maison du Seigneur.
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Et il envoya Eliacim qui était intendant dans la maison, et Sobna, le scribe, et les plus anciens d’entre les prêtres, couverts de sacs, vers Isaïe, le prophète, fils d’Amos,
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
Et ils lui dirent: Voici ce qu’a dit Ezéchias: Jour de tribulation, de reproche et de blasphème, est ce jour-ci, parce que des enfants sont venus jusqu’à l’enfantement, et la force manque à la mère pour enfanter.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
Peut-être que le Seigneur ton Dieu entendra les paroles de Rabsacès qu’a envoyé le roi des Assyriens son maître pour blasphémer le Dieu vivant, et pour l’insulter par les paroles qu’a entendues le Seigneur ton Dieu; fais donc monter une prière pour les restes qui ont été retrouvés.
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
Et les serviteurs du roi Ezéchias vinrent vers Isaïe,
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
Et Isaïe leur dit: Vous direz ceci à votre maître: Voici ce que dit le Seigneur: Ne crains point à cause des paroles que tu as entendues, par lesquelles m’ont blasphémé les serviteurs du roi des Assyriens.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Voilà que moi je lui enverrai un esprit de frayeur; il apprendra une nouvelle, et il retournera dans sa terre, et je le ferai tomber par le glaive dans sa terre.
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
Or Rabsacès s’en retourna, et trouva le roi des Assyriens formant le siège de Lobna. Car il avait appris qu’il était parti de Lachis,
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
Et Sennachérib entendit, au sujet de Tharaca, roi d’Ethiopie, des gens disant: Il est sorti pour combattre contre vous. Ce qu’ayant entendu, il envoya des messagers à Ezéchias, en disant:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
Vous direz ceci à Ezéchias, roi de Juda: Qu’il ne vous trompe pas, votre Dieu, en qui vous vous confiez, disant: Jérusalem, ne sera pas livrée à la main du roi des Assyriens.
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
Voilà que vous-même vous avez appris tout ce qu’ont fait les rois des Assyriens à tous les pays qu’ils ont détruits; et vous, vous pourrez échapper?
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
Est-ce que les dieux des nations ont délivré ceux qu’ont détruits mes pères, c’est-à-dire Gozam, et Haram, et Réseph, et les fils d’Eden qui étaient en Thalassar?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Où est le roi d’Emath, et le roi d’Arphad, et le roi de la ville de Sépharvaïm, d’Ana et d’Ava?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
Et Ezéchias reçut les livres de la main des messagers, et les lut, et il monta à la maison du Seigneur, et Ezéchias les étendit devant le Seigneur.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
Et Ezéchias pria le Seigneur, disant:
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Seigneur des armées, Dieu d’Israël, qui êtes assis sur les chérubins, c’est vous qui êtes seul Dieu de tous les royaumes de la terre, c’est vous qui avez fait le ciel et la terre.
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
Inclinez, Seigneur, votre oreille, et écoutez; ouvrez, Seigneur, vos yeux, et voyez, et écoutez toutes les paroles de Sennachérib, qu’il a envoyées pour blasphémer le Dieu vivant.
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
Car il est vrai, Seigneur, les rois des Assyriens ont rendu déserts les pays et leurs contrées.
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
Ils ont jeté leurs dieux au feu; car ce n’étaient pas des dieux, mais des ouvrages de mains d’hommes, du bois et de la pierre; et ils les ont mis en pièces.
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
Et maintenant, Seigneur notre Dieu, sauvez-nous de sa main; et qu’ils sachent, tous les royaumes de la terre, que c’est vous qui êtes le seul Seigneur.
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
Et Isaïe, fils d’Amos, envoya vers Ezéchias, disant: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d’Israël: À l’égard de ce que tu m’as demandé touchant Sennachérib, roi d’Assyrie,
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
Voici la parole que le Seigneur a dite à son sujet: Elle t’a méprisé, et elle t’a raillé, la vierge, fille de Sion; derrière toi elle a secoué la tête, la fille de Jérusalem.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
Qui as-tu insulté, qui as-tu blasphémé, et contre qui as-tu élevé la voix, et porté en haut tes yeux? Contre le saint d’Israël.
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
Par l’entremise de tes serviteurs tu as insulté le Seigneur, et tu as dit: Avec la multitude de mes quadriges, moi je suis monté sur la hauteur des montagnes, les chaînes du Liban; je couperai les cimes de ses cèdres, et ses plus beaux sapins, et je pénétrerai jusqu’à la pointe de son sommet, jusqu’à la forêt de son Carmel.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
C’est moi qui ai creusé des sources, et j’ai bu de l’eau, et j’ai séché par la trace de mon pied toutes les rivières retenues par des digues.
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
N’as-tu donc pas ouï dire les choses qu’autrefois j’y ai faites? dès les temps anciens, c’est moi qui ai disposé cela; et maintenant je l’ai amené et accompli en détruisant les collines qui s’entrechoquent et les cités fortifiées.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
Leurs habitants, à la main raccourcie, ont tremblé et ont été confondus; ils sont devenus comme le foin d’un champ et le gazon d’un pâturage, et l’herbe des toits, qui a séché avant qu’elle fût mûre.
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
Ton habitation, et ta sortie, et ton entrée, je les ai connues, ainsi que ta fureur extravagante contre moi.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
Lorsque tu étais furieux contre moi, ton orgueil est monté à mes oreilles; je mettrai donc un cercle à tes narines, et un mors à ta bouche, et je te ramènerai par la voie par laquelle tu es venu.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
Mais pour toi, Ezéchias, voici un signe: Mange cette année de ce qui naîtra de soi-même, et en la seconde année nourris-toi de fruits; mais en la troisième année, semez et moissonnez, et plantez des vignes, et mangez-en le fruit.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
Et ce qui sera sauvé de la maison de Juda, et ce qui est resté, jettera racine en bas, et fera du fruit en haut;
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
Parce que de Jérusalem sortiront des restes, et ce qui sera sauvé de la montagne de Sion; le zèle du Seigneur des armées fera cela.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur du roi des Assyriens: Il n’entrera pas dans cette cité, il n’y lancera pas de flèche, et pas un bouclier ne l’occupera, et il n’élèvera pas de terrasse autour d’elle.
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
Il retournera par la voie par laquelle il est venu; il n’entrera pas dans cette cité, dit le Seigneur;
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
Et je protégerai cette cité, afin que je la sauve à cause de moi et à cause de David, mon serviteur.
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
Or un ange du Seigneur sortit et frappa dans le camp des Assyriens cent quatre-vingt-cinq mille hommes. On se leva le matin, et voici que tous étaient des corps de morts.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
Et il partit, et il s’en alla, et il retourna, Sennachérib, roi des Assyriens, et il habita à Ninive.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et il arriva que, comme il adorait dans le temple de Nesroch, son dieu, Adramélech et Sarasar ses fils le frappèrent du glaive et s’enfuirent dans la terre d’Ararat, et Asarhaddon son fils régna en sa place.

< Yesaya 37 >