< Yesaya 37 >

1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
And it happened that, when king Hezekiah had heard this, he rent his garments, and he wrapped himself in sackcloth, and he entered the house of the Lord.
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
And he sent Eliakim, who was over the house, and Shebna, the scribe, and the elders of the priests, covered with sackcloth, to Isaiah, the son of Amoz, the prophet.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
And they said to him: “Thus says Hezekiah: This day is a day of tribulation, and of rebuke, and of blasphemy. For the sons have arrived at the time for birth, but there is not enough strength to bring them forth.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
Perhaps, somehow, the Lord your God will hear the words of Rabshakeh, whom the king of the Assyrians, his lord, has sent to blaspheme the living God, and will rebuke the words that the Lord your God has heard. Therefore, lift up your prayers on behalf of the remnant which has been left behind.”
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
And so the servants of king Hezekiah went to Isaiah.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
And Isaiah said to them: “You shall say this to your lord: Thus says the Lord: Do not be afraid to face the words that you have heard, by which the servants of the king of the Assyrians blasphemed me.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Behold, I will send a spirit to him, and he will hear a message, and he will return to his own land. And I will cause him to fall by the sword, in his own land.”
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
Then Rabshakeh returned, and he found the king of the Assyrians fighting against Libnah. For he had heard that he had set out from Lachish.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
And he heard from Tirhakah, the king of Ethiopia: “He has gone forth so that he may fight against you.” And when he had heard this, he sent messengers to Hezekiah, saying:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
“You shall say this to Hezekiah, the king of Judah, saying: Do not let your God, in whom you trust, deceive you by saying: ‘Jerusalem will not be given into the hands of the king of the Assyrians.’
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
Behold, you have heard about all that the kings of the Assyrians have done to all the lands that they have conquered, and so, how can you be delivered?
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
Have the gods of the nations rescued those whom my fathers have conquered: Gozan, and Haran, and Rezeph, and the sons of Eden who were at Telassar?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Where is the king of Hamath and the king of Arpad, or the king of the city of Sepharvaim, or of Hena and Ivvah?”
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
And Hezekiah took the letter from the hand of the messengers, and he read it, and he went up to the house of the Lord, and Hezekiah spread it out in the sight of the Lord.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
And Hezekiah prayed to the Lord, saying:
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
“O Lord of hosts, the God of Israel who sits upon the Cherubim: you alone are God of all the kingdoms of the earth. You have made heaven and earth.
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
O Lord, incline your ear and listen. O Lord, open your eyes and see. And hear all the words of Sennacherib, which he has sent to blaspheme the living God.
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
For truly, O Lord, the kings of the Assyrians have laid waste to countries and territories.
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
And they have cast their gods into the fire. For these were not gods, but the works of men’s hands, of wood and of stone. And they broke them into pieces.
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
And now, O Lord our God, save us from his hand. And let all the kingdoms of the earth acknowledge that you alone are Lord.”
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
And Isaiah, the son of Amoz, sent to Hezekiah, saying: “Thus says the Lord, the God of Israel: Because of what you have prayed to me about Sennacherib, the king of the Assyrians,
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
this is the word that the Lord has spoken over him: The virgin daughter of Zion has despised you and mocked you. The daughter of Jerusalem has shaken her head at you.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
Whom have you insulted? And whom have you blasphemed? And against whom have you lifted up your voice and raised up your eyes on high? Against the Holy One of Israel!
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
By the hand of your servants, you have reproached the Lord. And you have said: ‘With a multitude of my four-horse chariots, I have ascended the heights of the mountains adjoining Lebanon. And I will cut down its lofty cedars and its choice pine trees. And I will reach the top of its summit, to the forest of its Carmel.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
I dug deep, and I drank water, and I dried up all the river banks with the sole of my foot.’
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Have you not heard what I have done to it in past times? In ancient times, I formed it. And now I have brought it forth. And it has been made so that the hills and the fortified cities would fight together, unto its destruction.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
Their inhabitants had unsteady hands. They trembled and were confused. They became like the plants of the field, and the grass of the pastures, and like the weeds on the rooftops, which wither before they are mature.
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
I know your habitation, and your arrival, and your departure, and your madness against me.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
When you became angry against me, your arrogance rose up to my ears. Therefore, I will place a ring in your nose, and a bit between your lips. And I will turn you back on the road by which you arrived.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
But this shall be a sign for you: Eat, in this year, whatever springs up on its own. And in the second year, eat fruits. But in the third year, sow and reap, and plant vineyards, and eat their fruit.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
And what will be saved from the house of Judah, and what is left behind, will form deep roots, and will bear high fruits.
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
For from Jerusalem, a remnant shall go forth, and salvation from mount Zion. The zeal of the Lord of hosts will accomplish this.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
For this reason, thus says the Lord about the king of the Assyrians: He will not enter this city, nor shoot an arrow into it, nor overtake it with a shield, nor dig a rampart all around it.
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
He will return on the road by which he arrived. And into this city, he will not enter, says the Lord.
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
And I will protect this city, so that I may save it for my own sake, and for the sake of David, my servant.”
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
Then the Angel of the Lord went forth and struck down, in the camp of the Assyrians, one hundred eighty-five thousand. And they arose in the morning, and behold, all these were dead bodies.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
And Sennacherib, the king of the Assyrians, departed and went away. And he returned and lived at Nineveh.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
And it happened that, as he was adoring his god in the temple of Nisroch, his sons, Adramelech and Sharezer, struck him with the sword. And they fled into the land of Ararat. And Esarhaddon, his son, reigned in his place.

< Yesaya 37 >