< Yesaya 37 >
1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
Manghai Hezekiah loh a yaak vaengah a himbai a phen, tlamhni te a bai tih BOEIPA im te a paan.
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Te vaengah a im om Eliakim neh cadaek Shebna, khosoih patong rhoek te tlamhni a khuk tih tonghma Amoz capa Isaiah taengla a tueih.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
Te vaengah a taengah, “Hezekiah loh citcai neh toelthamnah khohnin neh kokhahnah khohnin ni. Camoe om hamla a pha tih a cun ham thadueng a om pawt bangla ka om coeng.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
Khotawt Rabshakeh kah olka te Yahovah na Pathen loh a yaak khaming. Aka hing Pathen veet hamla a boei Assyria manghai loh anih te a tueih coeng. Te ol Yahovah na Pathen loh a yaak coeng dongah a tluung bitni. A meet aka om duen ham khaw thangthuinah neh thothueng laeh,” a ti,” a ti nauh.
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
Manghai Hezekiah kah sal rhoek te Isaiah taengla a pawk uh vaengah,
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
amih te Isaiah loh, “Na boei taengah thui pah BOEIPA loh, 'Te ol te rhih boeh, Assyria manghai taengca rhoek loh kai n'hliphen te na yaak uh coeng.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Anih te mueihla ka paek vaengah olthang a yaak vetih amah kho la mael bitni. Te vaengah anih te amah kho ah cunghang neh ka cungku sak bitni,’ a ti,” a ti nah.
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
Lakhish lamloh a nong te a yaak vaengah khotawt Rabshakeh khaw mael van dae Assyria manghai loh Libnah a vathoh thil te a hmuh.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
Kusah manghai Tirhakah te a yaak coeng lahko. Nang vathoh thil ham ha pawk coeng a ti lah ko. A yaak tangloeng vaengah tah Hezekiah taengla puencawn a tueih tih,
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
“Judah manghai Hezekiah te thui pah. 'Na pangtung thil na Pathen loh nang n'rhaithi boel saeh,’ ti nah. 'Jerusalem khaw Assyria manghai kut dongla pawk mahpawh,’ ti nah.
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
Assyria manghai rhoek loh diklai tom te a saii tih amih a thup te namah loh na yaak coeng dongah na loeih uh venim te.
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
A pa rhoek loh a phae Gozan, Haran, Rezeph neh Telassar kah Eden ca rhoek te amih kah namtom pathen loh a huul a?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Khamath manghai neh Arpad manghai, Sepharvaim khopuei, Hena neh Ivvah manghai te ta,” a ti nah.
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
Puencawn kut lamkah ca te Hezekiah loh a doe tih a tae. Te phoeiah BOEIPA im la cet tih BOEIPA mikhmuh ah Hezekiah loh a phaih.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
Hezekiah tah BOEIPA taengah thangthui tih,
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
caempuei BOEIPA Israel Pathen, namah loh cherubim na ngol thil tih, diklai ram boeih soah namah bueng Pathen coeng. Namah loh vaan neh diklai na saii.
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
BOEIPA na hna kaeng lamtah hnatun lah. BOEIPA aw na mik dai lamtah hmu van lah. Sennacherib ol te boeih ya van lah. Aka hing Pathen veet hamla hlang a tueih lah ko te.
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
Aw BOEIPA, Assyria manghai rhoek loh diklai boeih neh a khohmuen khaw a khah uh coeng.
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
Amih kah pathen te hmai ah a pup pah. Te te pathen moenih. Hlang kut kah bibi thing neh lungto mailai ni, te dongah te rhoek khaw milh uh.
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
Kaimih Pathen Yahovah loh kaimih he anih kut lamloh n'khang pawn saeh. Te vaengah diklai ram pum loh nang namah bueng te BOEIPA la m'ming uh saeh,” a ti nah.
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
Te dongah Amoz capa Isaiah loh Hezekiah te a tah tih, “Israel Pathen Yahovah loh, 'Assyria manghai Sennacherib kongah kai taengla na thangthui coeng,’ a ti.
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
He ol he BOEIPA loh anih ham ni a thui. Zion nu oila nang te n'hnoelrhoeng tih, n'tamdaeng. Nang hnukah Jerusalem nu loh lu a hinghuen.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
Unim na veet tih na hliphen dae? Unim ol na huel thil van dae na mik nen tah Israel kah a cim taengah a sang la na huel.
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
Na sal rhoek kah kut loh Boeipa namah te m'veet. Te vaengah ka leng te yet neh Lebanon hlaep kah tlang sang khaw kamah ka yoeng coeng. Lamphai thingsang neh hmaical thinghloe khaw ka top coeng. A khobawt hmuensang kah a cangphill cangngol duup khaw ka pha coeng.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
Kamah loh ka rhawt tih tui ka ok. Egypt sokko boeih ka kho kah khopha neh kak sak.
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Hlamat kum lamloh ka nuen te daengrhae daengkhoi la na ya pawt nim. Ka hlom tangtae te ka paan coeng he,” na ti. Te dongah cakrhuek khopuei rhoek khaw hlang aka hnuei lungkuk a thaek bangla na om coeng.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
Amih khosa rhoek kah a kut toi tih rhihyawp uh. Te dongah khohmuen kah baelhing khaw yahhat la om. Imphu kah sulrham, toian thingsuep neh canghli kah te khaw mawn loh a boh.
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
Na om van tih na hlah uh van mai. Na pawk te khaw ka ming ngawn dae kai taengah na tlai hae.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
Kai taengah na tlai neh na mongkawt te ka hna la ha pawk coeng. Te dongah ka thisum neh na hnarhong ah ka dueh vetih na ka ah ka kamrhui kam ban ni. Te vaengah nang te kam mael puei vetih longpuei ah na pongpa ni.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
Te phoeiah hekah he nang ham ah miknoek la om ni. Kum khat pong vetih a kum bae ah anboe te caak ham om. Tedae a kum thum dongah tawn lamtah at bal. Misur te phung lamtah a thaih te ca khaw ca kolo van.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
Judah imkhui kah rhalyong te khaw a thap vetih a laedil kah a yung aka sueng tah a hman ah a thaih cuen ni.
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
Te vaengah Jerusalem lamkah a meet neh Zion tlang lamkah rhalyong te khaw ha pawk ni. Te tlam te caempuei BOEIPA kah thatlainah loh a saii ni.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
Te ham te BOEIPA loh a thui tangloeng. Assyria manghai te he khopuei khuila kun pawt vetih thaltang pataeng kap mahpawh. photling nen khaw mah pawt vetih tanglung khaw lun thil mahpawh.
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
Ha pawk nah longpuei long te mael vetih he khopuei khuila ha kun mahpawh. BOEIPA kah olphong coeng ni.
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
He khopuei he ka tungaep vetih, kamah ham neh ka sal David ham ka khang ni.
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
Te dongah BOEIPA kah puencawn loh a paan tih Assyria rhaehhmuen ah thawng ya rhet thawng nga te a ngawn pah. Mincang a thoh uh vaengah tah amih te a rhok la boeih duek uh.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
Te daengah puen uh tih vik cet. Assyria manghai Sennacherib khaw mael tih Nineveh ah kho a sak.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
Amah a om vaengah a pathen Nisrock im te a bakop thil hatah a ca rhoi Adrammelech neh Sharezer loh cunghang neh a tloek rhoi. Te dongah amih rhoi teArarat kho la poeng rhoi tih ana pa yuengla a capa Esarhaddon te tloep manghai.