< Yesaya 36 >
1 Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
І сталося, чотирна́дцятого року царя Єзекії прийшов Санхері́в, цар асирійський, на всі укріплені Юдині міста, та й захопив їх.
2 Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
І послав асирійський цар великого ча́шника з Лахішу до Єрусалиму, до царя Єзекії, з великим ві́йськом, і він став при водово́ді горі́шнього ставу, на битій дорозі поля Валю́шників.
3 Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
І вийшов до нього Еліяким, син Хілкійїн, начальник палати, і писар Шевна, та Йоах, син Асафів, ка́нцлер.
4 Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
І сказав їм великий ча́шник: „Скажіть Єзекії: Отак сказав великий цар, цар асирійський: Що́ це за надія, на яку ти наді́єшся?
5 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
Чи ду́маєш ти, що слово уст, то вже рада та сила до війни? На ко́го тепер наді́єшся, що збунтувався проти мене?
6 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
Ось ти наді́явся опе́ртися на оту пола́ману очерети́ну, на Єгипет, що коли хто опира́ється на неї, то вона входить у долоню йому, і продірявлює її. Отакий фараон, цар єгипетський, для всіх, хто наді́ється на нього!
7 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
А коли ти скажеш мені: Ми наді́ємось на Господа, Бога нашого, то чи ж Він не той, що Єзекія повсо́вував па́гірки його та же́ртівники його, і сказав Юді та Єрусалимові: перед оцим тільки же́ртівником будете вклонятися?
8 “Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
А тепер увійди́ но в союз з моїм паном, асирійським царем, і я дам тобі дві тисячі ко́ней, якщо ти зможеш собі дати на них верхівці́в.
9 Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
І як же ти прожене́ш хоч одного намісника з найменших рабів мого пана? А ти собі наді́явся на Єгипет ради колесни́ць та верхівці́в!
10 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
Тепер же, чи без волі Господа прийшов я на цей край, щоб знищити його? Господь сказав був мені: „Піди на той край та й знищ його!“
11 Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
І сказав Еліяким, і Шевна та Йоах до великого ча́шника: „Говори до своїх рабів по-араме́йському, бо ми розуміємо, і не говори до нас но-юдейському в голос при тих людях, що на мурі“.
12 Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
І сказав великий ча́шник: „Чи пан мій послав мене говорити: ці слова до твого пана та до тебе? Хіба не до цих людей, що сидять на мурі, щоб із вами їсти свій кал та пити свою се́чу?“
13 Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
І став великий ча́шник, і кликнув гучним голосом по-юдейському, і сказав: „Послухайте слів великого царя, царя асирійського!
14 Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
Так сказав цар: Нехай не ду́рить вас Єзекі́я, бо він не зможе врятува́ти вас!
15 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
І нехай не запевня́є вас Єзекія Господом, говорячи: Рятуючи, врятує вас Господь, і не буде да́но цього міста в руку царя асирійського.
16 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
Не слухайте Єзекі́ї, бо так сказав цар асирійський: „Примиріться зо мною, та й вийдіть до мене, та й їжте кожен свій виноград та кожен фіґу свою, і пийте кожен воду зо своєї ко́панки,
17 mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
аж поки я не прийду́ й не візьму́ вас до кра́ю такого ж, як ваш край, до кра́ю збіжжя та виноградного соку, до краю хліба та виноградників.
18 “Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Щоб не намовив вас Єзекі́я, говорячи: Господь порятує нас! Чи врятували боги́ тих наро́дів, кожен свій край від руки асирійського царя?
19 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Де боги́ Хамату та Арпаду? Де боги Сефарваїму? І чи врятували вони Самарі́ю від моєї руки?
20 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
Котри́й з-поміж усіх богі́в цих країв урятував свій край від моєї руки, — то невже ж Господь урятує Єрусалим від моєї руки?“
21 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
І мовчали вони, і не відповіли́ ані сло́ва, бо це був нака́з царя, що сказав „Не відповідайте йому́!“
22 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.
І прийшов Еліяки́м, син Хілкійїн, начальник палати, і писар Шевна, і Йоах, Асафів син, канцлер, з розде́ртими ша́тами, до Єзекії, і доне́сли йому слова́ великого ча́шника.